< Psalms 75 >

1 For the Chief Musician. To the tune of “Do Not Destroy.” A Psalm by Asaph. A song. We give thanks to you, God. We give thanks, for your Name is near. Men tell about your wondrous works.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 When I choose the appointed time, I will judge blamelessly.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 The earth and all its inhabitants quake. I firmly hold its pillars. (Selah)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 I said to the arrogant, “Do not boast!” I said to the wicked, “Do not lift up the horn.
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Do not lift up your horn on high. Do not speak with a stiff neck.”
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 For neither from the east, nor from the west, nor yet from the south, comes exaltation.
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 But God is the judge. He puts down one, and lifts up another.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 For in the LORD’s hand there is a cup, full of foaming wine mixed with spices. He pours it out. Indeed the wicked of the earth drink and drink it to its very dregs.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 But I will declare this forever: I will sing praises to the God of Jacob.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 I will cut off all the horns of the wicked, but the horns of the righteous shall be lifted up.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Psalms 75 >