< Psalms 2 >

1 Why do the nations rage, and the peoples plot a vain thing?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 The kings of the earth take a stand, and the rulers take counsel together, against the LORD, and against his Anointed, saying,
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 “Let’s break their bonds apart, and cast their cords from us.”
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 He who sits in the heavens will laugh. The Lord will have them in derision.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Then he will speak to them in his anger, and terrify them in his wrath:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 “Yet I have set my King on my holy hill of Zion.”
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 I will tell of the decree: The LORD said to me, “You are my son. Today I have become your father.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Ask of me, and I will give the nations for your inheritance, the uttermost parts of the earth for your possession.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 You shall break them with a rod of iron. You shall dash them in pieces like a potter’s vessel.”
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Now therefore be wise, you kings. Be instructed, you judges of the earth.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Serve the LORD with fear, and rejoice with trembling.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Give sincere homage to the Son, lest he be angry, and you perish on the way, for his wrath will soon be kindled. Blessed are all those who take refuge in him.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Psalms 2 >