< Psalms 147 >

1 Praise the LORD, for it is good to sing praises to our God; for it is pleasant and fitting to praise him.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 The LORD builds up Jerusalem. He gathers together the outcasts of Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 He heals the broken in heart, and binds up their wounds.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 He counts the number of the stars. He calls them all by their names.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Great is our Lord, and mighty in power. His understanding is infinite.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 The LORD upholds the humble. He brings the wicked down to the ground.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Sing to the LORD with thanksgiving. Sing praises on the harp to our God,
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 who covers the sky with clouds, who prepares rain for the earth, who makes grass grow on the mountains.
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 He provides food for the livestock, and for the young ravens when they call.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 He does not delight in the strength of the horse. He takes no pleasure in the legs of a man.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 The LORD takes pleasure in those who fear him, in those who hope in his loving kindness.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Praise the LORD, Jerusalem! Praise your God, Zion!
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 For he has strengthened the bars of your gates. He has blessed your children within you.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 He makes peace in your borders. He fills you with the finest of the wheat.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 He sends out his commandment to the earth. His word runs very swiftly.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 He gives snow like wool, and scatters frost like ashes.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 He hurls down his hail like pebbles. Who can stand before his cold?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 He sends out his word, and melts them. He causes his wind to blow, and the waters flow.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 He shows his word to Jacob, his statutes and his ordinances to Israel.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 He has not done this for just any nation. They do not know his ordinances. Praise the LORD!
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 147 >