< Psalms 146 >

1 Praise the LORD! Praise the LORD, my soul.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 While I live, I will praise the LORD. I will sing praises to my God as long as I exist.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Do not put your trust in princes, in a son of man in whom there is no help.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 His spirit departs, and he returns to the earth. In that very day, his thoughts perish.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Happy is he who has the God of Jacob for his help, whose hope is in the LORD, his God,
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 who made heaven and earth, the sea, and all that is in them; who keeps truth forever;
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 who executes justice for the oppressed; who gives food to the hungry. The LORD frees the prisoners.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 The LORD opens the eyes of the blind. The LORD raises up those who are bowed down. The LORD loves the righteous.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 The LORD preserves the foreigners. He upholds the fatherless and widow, but he turns the way of the wicked upside down.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 The LORD will reign forever; your God, O Zion, to all generations. Praise the LORD!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Psalms 146 >