< Psalms 135 >

1 Praise the LORD! Praise the LORD’s name! Praise him, you servants of the LORD,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 you who stand in the LORD’s house, in the courts of our God’s house.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Praise the LORD, for the LORD is good. Sing praises to his name, for that is pleasant.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 For the LORD has chosen Jacob for himself, Israel for his own possession.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 For I know that the LORD is great, that our Lord is above all gods.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Whatever the LORD pleased, that he has done, in heaven and in earth, in the seas and in all deeps.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 He causes the clouds to rise from the ends of the earth. He makes lightnings with the rain. He brings the wind out of his treasuries.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 He struck the firstborn of Egypt, both of man and animal.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 He sent signs and wonders into the middle of you, Egypt, on Pharaoh, and on all his servants.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 He struck many nations, and killed mighty kings—
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon king of the Amorites, Og king of Bashan, and all the kingdoms of Canaan—
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 and gave their land for a heritage, a heritage to Israel, his people.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Your name, LORD, endures forever; your renown, LORD, throughout all generations.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 For the LORD will judge his people and have compassion on his servants.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 The idols of the nations are silver and gold, the work of men’s hands.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 They have mouths, but they cannot speak. They have eyes, but they cannot see.
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 They have ears, but they cannot hear, neither is there any breath in their mouths.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Those who make them will be like them, yes, everyone who trusts in them.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 House of Israel, praise the LORD! House of Aaron, praise the LORD!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 House of Levi, praise the LORD! You who fear the LORD, praise the LORD!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Blessed be the LORD from Zion, who dwells in Jerusalem. Praise the LORD!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 135 >