< Psalms 13 >

1 For the Chief Musician. A Psalm by David. How long, LORD? Will you forget me forever? How long will you hide your face from me?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2 How long shall I take counsel in my soul, having sorrow in my heart every day? How long shall my enemy triumph over me?
Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3 Behold, and answer me, LORD, my God. Give light to my eyes, lest I sleep in death;
Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4 lest my enemy say, “I have prevailed against him;” lest my adversaries rejoice when I fall.
mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5 But I trust in your loving kindness. My heart rejoices in your salvation.
Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6 I will sing to the LORD, because he has been good to me.
Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.

< Psalms 13 >