< Psalms 127 >

1 A Song of Ascents. By Solomon. Unless the LORD builds the house, they who build it labor in vain. Unless the LORD watches over the city, the watchman guards it in vain.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
2 It is vain for you to rise up early, to stay up late, eating the bread of toil, for he gives sleep to his loved ones.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3 Behold, children are a heritage of the LORD. The fruit of the womb is his reward.
Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4 As arrows in the hand of a mighty man, so are the children of youth.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
5 Happy is the man who has his quiver full of them. They will not be disappointed when they speak with their enemies in the gate.
Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

< Psalms 127 >