< Psalms 119 >

1 ALEPH Blessed are those whose ways are blameless, who walk according to the LORD’s law.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Blessed are those who keep his statutes, who seek him with their whole heart.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Yes, they do nothing wrong. They walk in his ways.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 You have commanded your precepts, that we should fully obey them.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Oh that my ways were steadfast to obey your statutes!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Then I would not be disappointed, when I consider all of your commandments.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 I will give thanks to you with uprightness of heart, when I learn your righteous judgments.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 I will observe your statutes. Do not utterly forsake me.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 BETH How can a young man keep his way pure? By living according to your word.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 With my whole heart I have sought you. Do not let me wander from your commandments.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 I have hidden your word in my heart, that I might not sin against you.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Blessed are you, LORD. Teach me your statutes.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 With my lips, I have declared all the ordinances of your mouth.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 I have rejoiced in the way of your testimonies, as much as in all riches.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 I will meditate on your precepts, and consider your ways.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 I will delight myself in your statutes. I will not forget your word.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 GIMEL Do good to your servant. I will live and I will obey your word.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Open my eyes, that I may see wondrous things out of your law.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 I am a stranger on the earth. Do not hide your commandments from me.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 My soul is consumed with longing for your ordinances at all times.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 You have rebuked the proud who are cursed, who wander from your commandments.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Take reproach and contempt away from me, for I have kept your statutes.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Though princes sit and slander me, your servant will meditate on your statutes.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Indeed your statutes are my delight, and my counselors.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 DALETH My soul is laid low in the dust. Revive me according to your word!
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 I declared my ways, and you answered me. Teach me your statutes.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Let me understand the teaching of your precepts! Then I will meditate on your wondrous works.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 My soul is weary with sorrow; strengthen me according to your word.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Keep me from the way of deceit. Grant me your law graciously!
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 I have chosen the way of truth. I have set your ordinances before me.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 I cling to your statutes, LORD. Do not let me be disappointed.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 I run in the path of your commandments, for you have set my heart free.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 HE Teach me, LORD, the way of your statutes. I will keep them to the end.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Give me understanding, and I will keep your law. Yes, I will obey it with my whole heart.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Direct me in the path of your commandments, for I delight in them.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Turn my heart toward your statutes, not toward selfish gain.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Turn my eyes away from looking at worthless things. Revive me in your ways.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Fulfill your promise to your servant, that you may be feared.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Take away my disgrace that I dread, for your ordinances are good.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Behold, I long for your precepts! Revive me in your righteousness.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 VAV Let your loving kindness also come to me, LORD, your salvation, according to your word.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 So I will have an answer for him who reproaches me, for I trust in your word.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Do not snatch the word of truth out of my mouth, for I put my hope in your ordinances.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 So I will obey your law continually, forever and ever.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 I will walk in liberty, for I have sought your precepts.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 I will also speak of your statutes before kings, and will not be disappointed.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 I will delight myself in your commandments, because I love them.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 I reach out my hands for your commandments, which I love. I will meditate on your statutes.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 ZAYIN Remember your word to your servant, because you gave me hope.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 This is my comfort in my affliction, for your word has revived me.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 The arrogant mock me excessively, but I do not swerve from your law.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 I remember your ordinances of old, LORD, and have comforted myself.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Indignation has taken hold on me, because of the wicked who forsake your law.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Your statutes have been my songs in the house where I live.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 I have remembered your name, LORD, in the night, and I obey your law.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 This is my way, that I keep your precepts.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 HETH The LORD is my portion. I promised to obey your words.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 I sought your favor with my whole heart. Be merciful to me according to your word.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 I considered my ways, and turned my steps to your statutes.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 I will hurry, and not delay, to obey your commandments.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 The ropes of the wicked bind me, but I will not forget your law.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 At midnight I will rise to give thanks to you, because of your righteous ordinances.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 I am a friend of all those who fear you, of those who observe your precepts.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 The earth is full of your loving kindness, LORD. Teach me your statutes.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 TETH You have treated your servant well, according to your word, LORD.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Teach me good judgment and knowledge, for I believe in your commandments.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Before I was afflicted, I went astray; but now I observe your word.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 You are good, and do good. Teach me your statutes.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 The proud have smeared a lie upon me. With my whole heart, I will keep your precepts.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Their heart is as callous as the fat, but I delight in your law.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 It is good for me that I have been afflicted, that I may learn your statutes.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 The law of your mouth is better to me than thousands of pieces of gold and silver.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 YODH Your hands have made me and formed me. Give me understanding, that I may learn your commandments.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Those who fear you will see me and be glad, because I have put my hope in your word.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 LORD, I know that your judgments are righteous, that in faithfulness you have afflicted me.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Please let your loving kindness be for my comfort, according to your word to your servant.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Let your tender mercies come to me, that I may live; for your law is my delight.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Let the proud be disappointed, for they have overthrown me wrongfully. I will meditate on your precepts.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Let those who fear you turn to me. They will know your statutes.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Let my heart be blameless toward your decrees, that I may not be disappointed.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 KAPF My soul faints for your salvation. I hope in your word.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 My eyes fail for your word. I say, “When will you comfort me?”
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 For I have become like a wineskin in the smoke. I do not forget your statutes.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 How many are the days of your servant? When will you execute judgment on those who persecute me?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 The proud have dug pits for me, contrary to your law.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 All of your commandments are faithful. They persecute me wrongfully. Help me!
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 They had almost wiped me from the earth, but I did not forsake your precepts.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Preserve my life according to your loving kindness, so I will obey the statutes of your mouth.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 LAMEDH LORD, your word is settled in heaven forever.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Your faithfulness is to all generations. You have established the earth, and it remains.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Your laws remain to this day, for all things serve you.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Unless your law had been my delight, I would have perished in my affliction.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 I will never forget your precepts, for with them, you have revived me.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 I am yours. Save me, for I have sought your precepts.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 The wicked have waited for me, to destroy me. I will consider your statutes.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 I have seen a limit to all perfection, but your commands are boundless.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 MEM How I love your law! It is my meditation all day.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Your commandments make me wiser than my enemies, for your commandments are always with me.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 I have more understanding than all my teachers, for your testimonies are my (meditation)
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 I understand more than the aged, because I have kept your precepts.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 I have kept my feet from every evil way, that I might observe your word.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 I have not turned away from your ordinances, for you have taught me.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 How sweet are your promises to my taste, more than honey to my mouth!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Through your precepts, I get understanding; therefore I hate every false way.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 NUN Your word is a lamp to my feet, and a light for my path.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 I have sworn, and have confirmed it, that I will obey your righteous ordinances.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 I am afflicted very much. Revive me, LORD, according to your word.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Accept, I beg you, the willing offerings of my mouth. LORD, teach me your ordinances.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 My soul is continually in my hand, yet I will not forget your law.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 The wicked have laid a snare for me, yet I have not gone astray from your precepts.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 I have taken your testimonies as a heritage forever, for they are the joy of my heart.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 I have set my heart to perform your statutes forever, even to the end.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 SAMEKH I hate double-minded men, but I love your law.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 You are my hiding place and my shield. I hope in your word.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Depart from me, you evildoers, that I may keep the commandments of my God.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Uphold me according to your word, that I may live. Let me not be ashamed of my hope.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Hold me up, and I will be safe, and will have respect for your statutes continually.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 You reject all those who stray from your statutes, for their deceit is in vain.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 You put away all the wicked of the earth like dross. Therefore I love your testimonies.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 My flesh trembles for fear of you. I am afraid of your judgments.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 AYIN I have done what is just and righteous. Do not leave me to my oppressors.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Ensure your servant’s well-being. Do not let the proud oppress me.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 My eyes fail looking for your salvation, for your righteous word.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Deal with your servant according to your loving kindness. Teach me your statutes.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 I am your servant. Give me understanding, that I may know your testimonies.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 It is time to act, LORD, for they break your law.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Therefore I love your commandments more than gold, yes, more than pure gold.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Therefore I consider all of your precepts to be right. I hate every false way.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 PE Your testimonies are wonderful, therefore my soul keeps them.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 The entrance of your words gives light. It gives understanding to the simple.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 I opened my mouth wide and panted, for I longed for your commandments.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Turn to me, and have mercy on me, as you always do to those who love your name.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Establish my footsteps in your word. Do not let any iniquity have dominion over me.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Redeem me from the oppression of man, so I will observe your precepts.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Make your face shine on your servant. Teach me your statutes.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Streams of tears run down my eyes, because they do not observe your law.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 TZADHE You are righteous, LORD. Your judgments are upright.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 You have commanded your statutes in righteousness. They are fully trustworthy.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 My zeal wears me out, because my enemies ignore your words.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Your promises have been thoroughly tested, and your servant loves them.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 I am small and despised. I do not forget your precepts.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Your righteousness is an everlasting righteousness. Your law is truth.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Trouble and anguish have taken hold of me. Your commandments are my delight.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Your testimonies are righteous forever. Give me understanding, that I may live.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 QOPH I have called with my whole heart. Answer me, LORD! I will keep your statutes.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 I have called to you. Save me! I will obey your statutes.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 I rise before dawn and cry for help. I put my hope in your words.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 My eyes stay open through the night watches, that I might meditate on your word.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Hear my voice according to your loving kindness. Revive me, LORD, according to your ordinances.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 They draw near who follow after wickedness. They are far from your law.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 You are near, LORD. All your commandments are truth.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Of old I have known from your testimonies, that you have founded them forever.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 RESH Consider my affliction, and deliver me, for I do not forget your law.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Plead my cause, and redeem me! Revive me according to your promise.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Salvation is far from the wicked, for they do not seek your statutes.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Great are your tender mercies, LORD. Revive me according to your ordinances.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Many are my persecutors and my adversaries. I have not swerved from your testimonies.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 I look at the faithless with loathing, because they do not observe your word.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Consider how I love your precepts. Revive me, LORD, according to your loving kindness.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 All of your words are truth. Every one of your righteous ordinances endures forever.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 SIN AND SHIN Princes have persecuted me without a cause, but my heart stands in awe of your words.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 I rejoice at your word, as one who finds great plunder.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 I hate and abhor falsehood. I love your law.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Seven times a day, I praise you, because of your righteous ordinances.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Those who love your law have great peace. Nothing causes them to stumble.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 I have hoped for your salvation, LORD. I have done your commandments.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 My soul has observed your testimonies. I love them exceedingly.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 I have obeyed your precepts and your testimonies, for all my ways are before you.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 TAV Let my cry come before you, LORD. Give me understanding according to your word.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Let my supplication come before you. Deliver me according to your word.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Let my lips utter praise, for you teach me your statutes.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Let my tongue sing of your word, for all your commandments are righteousness.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Let your hand be ready to help me, for I have chosen your precepts.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 I have longed for your salvation, LORD. Your law is my delight.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Let my soul live, that I may praise you. Let your ordinances help me.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 I have gone astray like a lost sheep. Seek your servant, for I do not forget your commandments.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalms 119 >