< Psalms 104 >

1 Bless the LORD, my soul. The LORD, my God, you are very great. You are clothed with honor and majesty.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 He covers himself with light as with a garment. He stretches out the heavens like a curtain.
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 He lays the beams of his rooms in the waters. He makes the clouds his chariot. He walks on the wings of the wind.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 He makes his messengers winds, and his servants flames of fire.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 He laid the foundations of the earth, that it should not be moved forever.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 You covered it with the deep as with a cloak. The waters stood above the mountains.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 At your rebuke they fled. At the voice of your thunder they hurried away.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 The mountains rose, the valleys sank down, to the place which you had assigned to them.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 You have set a boundary that they may not pass over, that they do not turn again to cover the earth.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 He sends springs into the valleys. They run among the mountains.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 They give drink to every animal of the field. The wild donkeys quench their thirst.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 The birds of the sky nest by them. They sing among the branches.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 He waters the mountains from his rooms. The earth is filled with the fruit of your works.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 He causes the grass to grow for the livestock, and plants for man to cultivate, that he may produce food out of the earth:
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 wine that makes the heart of man glad, oil to make his face to shine, and bread that strengthens man’s heart.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 The LORD’s trees are well watered, the cedars of Lebanon, which he has planted,
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 where the birds make their nests. The stork makes its home in the cypress trees.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 The high mountains are for the wild goats. The rocks are a refuge for the rock badgers.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 He appointed the moon for seasons. The sun knows when to set.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 You make darkness, and it is night, in which all the animals of the forest prowl.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 The young lions roar after their prey, and seek their food from God.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 The sun rises, and they steal away, and lie down in their dens.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Man goes out to his work, to his labor until the evening.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 LORD, how many are your works! In wisdom, you have made them all. The earth is full of your riches.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 There is the sea, great and wide, in which are innumerable living things, both small and large animals.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 There the ships go, and leviathan, whom you formed to play there.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 These all wait for you, that you may give them their food in due season.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 You give to them; they gather. You open your hand; they are satisfied with good.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 You hide your face; they are troubled. You take away their breath; they die and return to the dust.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 You send out your Spirit and they are created. You renew the face of the ground.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Let the LORD’s glory endure forever. Let the LORD rejoice in his works.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 He looks at the earth, and it trembles. He touches the mountains, and they smoke.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 I will sing to the LORD as long as I live. I will sing praise to my God while I have any being.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Let my meditation be sweet to him. I will rejoice in the LORD.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Let sinners be consumed out of the earth. Let the wicked be no more. Bless the LORD, my soul. Praise the LORD!
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psalms 104 >