< Psalms 103 >

1 By David. Praise the LORD, my soul! All that is within me, praise his holy name!
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 Praise the LORD, my soul, and do not forget all his benefits,
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 who forgives all your sins, who heals all your diseases,
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 who redeems your life from destruction, who crowns you with loving kindness and tender mercies,
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 who satisfies your desire with good things, so that your youth is renewed like the eagle’s.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 The LORD executes righteous acts, and justice for all who are oppressed.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 He made known his ways to Moses, his deeds to the children of Israel.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 The LORD is merciful and gracious, slow to anger, and abundant in loving kindness.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 He will not always accuse; neither will he stay angry forever.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 He has not dealt with us according to our sins, nor repaid us for our iniquities.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 For as the heavens are high above the earth, so great is his loving kindness toward those who fear him.
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 As far as the east is from the west, so far has he removed our transgressions from us.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 Like a father has compassion on his children, so the LORD has compassion on those who fear him.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 For he knows how we are made. He remembers that we are dust.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 As for man, his days are like grass. As a flower of the field, so he flourishes.
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 For the wind passes over it, and it is gone. Its place remembers it no more.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 But the LORD’s loving kindness is from everlasting to everlasting with those who fear him, his righteousness to children’s children,
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 to those who keep his covenant, to those who remember to obey his precepts.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 The LORD has established his throne in the heavens. His kingdom rules over all.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Praise the LORD, you angels of his, who are mighty in strength, who fulfill his word, obeying the voice of his word.
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Praise the LORD, all you armies of his, you servants of his, who do his pleasure.
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Praise the LORD, all you works of his, in all places of his dominion. Praise the LORD, my soul!
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

< Psalms 103 >