< Luke 1 >

1 Since many have undertaken to set in order a narrative concerning those matters which have been fulfilled among us,
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
2 even as those who from the beginning were eyewitnesses and servants of the word delivered them to us,
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 it seemed good to me also, having traced the course of all things accurately from the first, to write to you in order, most excellent Theophilus;
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 that you might know the certainty concerning the things in which you were instructed.
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 There was in the days of Herod, the king of Judea, a certain priest named Zacharias, of the priestly division of Abijah. He had a wife of the daughters of Aaron, and her name was Elizabeth.
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 They were both righteous before God, walking blamelessly in all the commandments and ordinances of the Lord.
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 But they had no child, because Elizabeth was barren, and they both were well advanced in years.
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 Now while he executed the priest’s office before God in the order of his division
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 according to the custom of the priest’s office, his lot was to enter into the temple of the Lord and burn incense.
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 The whole multitude of the people were praying outside at the hour of incense.
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 An angel of the Lord appeared to him, standing on the right side of the altar of incense.
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 Zacharias was troubled when he saw him, and fear fell upon him.
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 But the angel said to him, “Do not be afraid, Zacharias, because your request has been heard. Your wife, Elizabeth, will bear you a son, and you shall call his name John.
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 You will have joy and gladness, and many will rejoice at his birth.
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 For he will be great in the sight of the Lord, and he will drink no wine nor strong drink. He will be filled with the Holy Spirit, even from his mother’s womb.
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 He will turn many of the children of Israel to the Lord their God.
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 He will go before him in the spirit and power of Elijah, ‘to turn the hearts of the fathers to the children,’ and the disobedient to the wisdom of the just; to prepare a people prepared for the Lord.”
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 Zacharias said to the angel, “How can I be sure of this? For I am an old man, and my wife is well advanced in years.”
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 The angel answered him, “I am Gabriel, who stands in the presence of God. I was sent to speak to you and to bring you this good news.
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 Behold, you will be silent and not able to speak until the day that these things will happen, because you did not believe my words, which will be fulfilled in their proper time.”
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 The people were waiting for Zacharias, and they marveled that he delayed in the temple.
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 When he came out, he could not speak to them. They perceived that he had seen a vision in the temple. He continued making signs to them, and remained mute.
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 When the days of his service were fulfilled, he departed to his house.
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 After these days Elizabeth his wife conceived, and she hid herself five months, saying,
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 “Thus has the Lord done to me in the days in which he looked at me, to take away my reproach among men.”
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 Now in the sixth month, the angel Gabriel was sent from God to a city of Galilee named Nazareth,
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 to a virgin pledged to be married to a man whose name was Joseph, of David’s house. The virgin’s name was Mary.
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 Having come in, the angel said to her, “Rejoice, you highly favored one! The Lord is with you. Blessed are you among women!”
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 But when she saw him, she was greatly troubled at the saying, and considered what kind of salutation this might be.
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 The angel said to her, “Do not be afraid, Mary, for you have found favor with God.
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 Behold, you will conceive in your womb and give birth to a son, and shall name him ‘Jesus.’
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 He will be great and will be called the Son of the Most High. The Lord God will give him the throne of his father David,
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 and he will reign over the house of Jacob for the ages (aiōn g165). There will be no end to his Kingdom."
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
34 Mary said to the angel, “How can this be, seeing I am a virgin?”
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 The angel answered her, “The Holy Spirit will come on you, and the power of the Most High will overshadow you. Therefore also the holy one who is born from you will be called the Son of God.
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 Behold, Elizabeth your relative also has conceived a son in her old age; and this is the sixth month with her who was called barren.
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 For nothing spoken by God is impossible.”
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 Mary said, “Behold, the servant of the Lord; let it be done to me according to your word.” Then the angel departed from her.
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 Mary arose in those days and went into the hill country with haste, into a city of Judah,
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 and entered into the house of Zacharias and greeted Elizabeth.
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 When Elizabeth heard Mary’s greeting, the baby leaped in her womb; and Elizabeth was filled with the Holy Spirit.
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 She called out with a loud voice and said, “Blessed are you among women, and blessed is the fruit of your womb!
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 Why am I so favored, that the mother of my Lord should come to me?
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 For behold, when the voice of your greeting came into my ears, the baby leaped in my womb for joy!
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 Blessed is she who believed, for there will be a fulfillment of the things which have been spoken to her from the Lord!”
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 Mary said, “My soul magnifies the Lord.
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 My spirit has rejoiced in God my Savior,
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 for he has looked at the humble state of his servant. For behold, from now on, all generations will call me blessed.
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 For he who is mighty has done great things for me. Holy is his name.
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 His mercy is for generations and generations on those who fear him.
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 He has shown strength with his arm. He has scattered the proud in the imagination of their hearts.
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 He has put down princes from their thrones, and has exalted the lowly.
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 He has filled the hungry with good things. He has sent the rich away empty.
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 He has given help to Israel, his servant, that he might remember mercy,
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 as he spoke to our fathers, to Abraham and his offspring for the age (aiōn g165)."
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
56 Mary stayed with her about three months, and then returned to her house.
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 Now the time that Elizabeth should give birth was fulfilled, and she gave birth to a son.
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 Her neighbors and her relatives heard that the Lord had magnified his mercy toward her, and they rejoiced with her.
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 On the eighth day, they came to circumcise the child; and they would have called him Zacharias, after the name of his father.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 His mother answered, “Not so; but he will be called John.”
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 They said to her, “There is no one among your relatives who is called by this name.”
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 They made signs to his father, what he would have him called.
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 He asked for a writing tablet, and wrote, “His name is John.” They all marveled.
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 His mouth was opened immediately and his tongue freed, and he spoke, blessing God.
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 Fear came on all who lived around them, and all these sayings were talked about throughout all the hill country of Judea.
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 All who heard them laid them up in their heart, saying, “What then will this child be?” The hand of the Lord was with him.
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 His father Zacharias was filled with the Holy Spirit, and prophesied, saying,
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 “Blessed be the Lord, the God of Israel, for he has visited and redeemed his people;
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 and has raised up a horn of salvation for us in the house of his servant David
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 (as he spoke by the mouth of his holy prophets who have been from the age (aiōn g165)),
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
71 salvation from our enemies and from the hand of all who hate us;
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 to show mercy toward our fathers, to remember his holy covenant,
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 the oath which he swore to Abraham our father,
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 to grant to us that we, being delivered out of the hand of our enemies, should serve him without fear,
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 in holiness and righteousness before him all the days of our life.
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 And you, child, will be called a prophet of the Most High; for you will go before the face of the Lord to prepare his ways,
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 to give knowledge of salvation to his people by the remission of their sins,
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 because of the tender mercy of our God, by which the dawn from on high will visit us,
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 to shine on those who sit in darkness and the shadow of death; to guide our feet into the way of peace.”
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 The child was growing and becoming strong in spirit, and was in the desert until the day of his public appearance to Israel.
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.

< Luke 1 >