< Luke 18 >

1 He also spoke a parable to them that they must always pray and not give up,
Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
2 saying, “There was a judge in a certain city who did not fear God and did not respect man.
Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
3 A widow was in that city, and she often came to him, saying, ‘Defend me from my adversary!’
Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
4 He would not for a while; but afterward he said to himself, ‘Though I neither fear God nor respect man,
“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
5 yet because this widow bothers me, I will defend her, or else she will wear me out by her continual coming.’”
koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
6 The Lord said, “Listen to what the unrighteous judge says.
Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
7 Will not God avenge his chosen ones who are crying out to him day and night, and yet he exercises patience with them?
Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
8 I tell you that he will avenge them quickly. Nevertheless, when the Son of Man comes, will he find faith on the earth?”
Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
9 He also spoke this parable to certain people who were convinced of their own righteousness, and who despised all others:
Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
10 “Two men went up into the temple to pray; one was a Pharisee, and the other was a tax collector.
“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
11 The Pharisee stood and prayed by himself like this: ‘God, I thank you that I am not like the rest of men: extortionists, unrighteous, adulterers, or even like this tax collector.
Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
12 I fast twice a week. I give tithes of all that I get.’
Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
13 But the tax collector, standing far away, would not even lift up his eyes to heaven, but beat his chest, saying, ‘God, be merciful to me, a sinner!’
“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
14 I tell you, this man went down to his house justified rather than the other; for everyone who exalts himself will be humbled, but he who humbles himself will be exalted.”
“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
15 They were also bringing their babies to him, that he might touch them. But when the disciples saw it, they rebuked them.
Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
16 Jesus summoned them, saying, “Allow the little children to come to me, and do not hinder them, for God’s Kingdom belongs to such as these.
Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
17 Most certainly, I tell you, whoever does not receive God’s Kingdom like a little child, he will in no way enter into it.”
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
18 A certain ruler asked him, saying, "Good Teacher, what shall I do to inherit consummate (aiōnios g166) life?"
Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
19 Jesus asked him, “Why do you call me good? No one is good, except one: God.
Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
20 You know the commandments: ‘Do not commit adultery,’ ‘Do not murder,’ ‘Do not steal,’ ‘Do not give false testimony,’ ‘Honor your father and your mother.’”
Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
21 He said, “I have observed all these things from my youth up.”
Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
22 When Jesus heard these things, he said to him, “You still lack one thing. Sell all that you have and distribute it to the poor. Then you will have treasure in heaven; then come, follow me.”
Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
23 But when he heard these things, he became very sad, for he was very rich.
Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
24 Jesus, seeing that he became very sad, said, “How hard it is for those who have riches to enter into God’s Kingdom!
Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
25 For it is easier for a camel to enter in through a needle’s eye than for a rich man to enter into God’s Kingdom.”
Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
26 Those who heard it said, “Then who can be saved?”
Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
27 But he said, “The things which are impossible with men are possible with God.”
Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
28 Peter said, “Look, we have left everything and followed you.”
Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
29 He said to them, “Most certainly I tell you, there is no one who has left house, or wife, or brothers, or parents, or children, for God’s Kingdom’s sake,
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
30 who will not receive many times more in this time, and in the age (aiōn g165) to come, consummate (aiōnios g166) life."
adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
31 He took the twelve aside and said to them, “Behold, we are going up to Jerusalem, and all the things that are written through the prophets concerning the Son of Man will be completed.
Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
32 For he will be delivered up to the Gentiles, will be mocked, treated shamefully, and spit on.
Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
33 They will scourge and kill him. On the third day, he will rise again.”
adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
34 They understood none of these things. This saying was hidden from them, and they did not understand the things that were said.
Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
35 As he came near Jericho, a certain blind man sat by the road, begging.
Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
36 Hearing a multitude going by, he asked what this meant.
anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
37 They told him that Jesus of Nazareth was passing by.
Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
38 He cried out, “Jesus, you son of David, have mercy on me!”
Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
39 Those who led the way rebuked him, that he should be quiet; but he cried out all the more, “You son of David, have mercy on me!”
Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
40 Standing still, Jesus commanded him to be brought to him. When he had come near, he asked him,
Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
41 “What do you want me to do?” He said, “Lord, that I may see again.”
“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
42 Jesus said to him, “Receive your sight. Your faith has healed you.”
Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
43 Immediately he received his sight and followed him, glorifying God. All the people, when they saw it, praised God.
Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.

< Luke 18 >