< Job 26 >

1 Then Job answered,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “How have you helped him who is without power! How have you saved the arm that has no strength!
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 How have you counseled him who has no wisdom, and plentifully declared sound knowledge!
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 To whom have you uttered words? Whose spirit came out of you?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 “The departed spirits tremble, those beneath the waters and all that live in them.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 Sheol (Sheol h7585) is naked before God, and Abaddon has no covering.
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 He stretches out the north over empty space, and hangs the earth on nothing.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 He binds up the waters in his thick clouds, and the cloud is not burst under them.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 He encloses the face of his throne, and spreads his cloud on it.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 He has described a boundary on the surface of the waters, and to the confines of light and darkness.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 The pillars of heaven tremble and are astonished at his rebuke.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 He stirs up the sea with his power, and by his understanding he strikes through Rahab.
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 By his Spirit the heavens are garnished. His hand has pierced the swift serpent.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 Behold, these are but the outskirts of his ways. How small a whisper do we hear of him! But the thunder of his power who can understand?”
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< Job 26 >