< Job 22 >

1 Weer nam Elifaz van Teman het woord, en sprak:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Handelt de mens soms ten bate van God? Neen, ten eigen bate is men wijs.
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Heeft de Almachtige er voordeel van, als ge vroom zijt, Of profijt, zo ge onberispelijk leeft?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Bestraft Hij u soms om uw godsvrucht, Daagt Hij u daarom voor het gerecht?
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Is het niet om uw grote boosheid, Om uw fouten, zonder eind?
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 Ja, zonder noodzaak neemt ge pand van uw broeders, En trekt de berooiden de kleren uit;
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 Den dorstige geeft ge geen water, Den hongerige onthoudt ge zijn brood.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 Den man met de vuist moet het land toebehoren, En de gunsteling moet het bewonen;
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 Maar de weduwen zendt ge zonder iets heen, De armen der wezen slaat ge stuk!
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 En daarom zijt ge van strikken omringd, Plotseling verbijsterd van schrik;
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 Is uw licht verduisterd, zodat ge niet ziet, Slaat de stortvloed over u heen!
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 Woont God niet hoog in de hemel? Zie eens, hoe hoog de sterren staan!
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Maar gij besluit er uit: Wat kan God weten, Of richten door de wolken heen?
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Het zwerk is een sluier voor Hem, zodat Hij niet ziet, Hij wandelt rond op het hemelgewelf.
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Wilt ge de weg van vroeger bewandelen Die de boosdoeners hebben betreden:
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 Die vóór hun tijd zijn weggesleurd, Toen de vloed hun grondvesten wegspoelde?
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 Die tot God durfden zeggen: Weg van ons! Wat kan de Almachtige ons doen?
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Hij had hun huizen met voorspoed gevuld, En Zich niet met de plannen der bozen bemoeid.
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 De vromen zien het met vreugde, De onschuldige drijft de spot met hen:
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 "Waarachtig, hun have vernield, Hun overvloed door het vuur verteerd!"
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 Verzoen u met Hem, dan leeft ge in vrede, Dan wordt uw rijkdom weer groot;
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Neem de onderrichting aan uit zijn mond, En bewaar zijn woord in uw hart.
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Wanneer ge vol ootmoed u tot den Almachtige bekeert, De ongerechtigheid uit uw tent verwijdert:
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Dan zult ge het goud als stof gaan schatten, Het Ofirgoud als kiezel der beken.
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Want de Almachtige zal het fijnste goud voor u zijn, En stapels van zilver;
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 Dan zult ge u in den Almachtige verlustigen, En uw aanschijn verheffen tot God.
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Dan zult ge Hem roepen: Hij zal u verhoren, En ge zult Hem dankoffers brengen;
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Onderneemt ge iets, het komt tot stand, En het licht zal uw wegen bestralen!
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Want Hij vernedert de trots, Maar redt, wie de ogen neerslaat;
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 Hij verlost den onschuldige: Door de reinheid uwer handen wordt ook gij dus verlost!
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

< Job 22 >