< Chiyubunuzyo 8 >

1 Lino mwana wambelele wakajula chijazyo chamusanu atubili, kwakaba kumunisya kujulu kwachipanzi chahola.
Atatsekula chomatira chachisanu ndi chiwiri, kumwamba kunakhala chete mphindi makumi atatu.
2 Mpawo ndakabona bangelo balimusanu ababili kabayimvwi kunembo lyaLeza amyeembo ilimusanu ayibili yakapegwa mbabo.
Ndipo ndinaona angelo asanu ndi awiri aja amene amayimirira pamaso pa Mulungu, akupatsidwa malipenga asanu ndi awiri.
3 Awumwi mungelo wakaza, kanyampwide kapeyili kangolida katununkilizyo, kayimvwi kuchipayilo chatununkilizyo. Tununkilizyo twiingi twakapegwa nguwe kuti atupe nkombyo yabantu baLeza boonse basalala achipayililo changolida kunembo lyachuuno chabulemu.
Mngelo wina amene anali ndi chofukizira chagolide anabwera nayimirira pa guwa lansembe. Anapatsidwa lubani wambiri kuti amupereke pamodzi ndi mapemphero a anthu onse oyera mtima pa guwa lansembe lagolide patsogolo pa mpando waufumu.
4 Busi bwatununkilizyo - ankombyo zaybantu baLeza basalala - bwakanyampuka kunembo lyaLeza kuzwa mumaboko amungelo.
Fungo la lubani pamodzi ndi mapemphero a oyera mtima zinakwera kumwamba kwa Mulungu kuchokera mʼdzanja la mngeloyo.
5 Mungelo wakabweza kapeyili katununkilizyo akukazuzya mulilo kuzwa achipayililo. Mpawo wakawalila ansi anyika, alimwi kwakali mpatumpatu zyandabe, mubbalubbal, kumweka kwatulabi, amuzuzumo wanyika.
Kenaka mngeloyo anatenga chofukizira nachidzaza ndi moto wochokera pa guwa lansembe ndi kuponya pa dziko lapansi ndipo nthawi yomweyo panachitika mabingu, phokoso, mphenzi ndi chivomerezi.
6 Bangelo balimusanu ababili bakali amyeembo ilimusana ayibili bakalibambila kuti bayilizye.
Angelo asanu ndi awiri anakonzekera kuyimba malipenga asanu ndi awiri.
7 Mungelo mutanzi wakalizya mweembo wakwe alimwi kwakaba bulmu amulilo uvwelene abulow. Wakabwalilwa ansi anyika, alimwi akuti chisela chatatu chawo chakawumpigwa. Chisela chatatu chamisamu chakawumpigwa, amasokwe matyetye woonse akumpigwa.
Mngelo woyamba anayimba lipenga lake ndipo kunabwera matalala ndi moto wosakanizana ndi magazi ndipo unaponyedwa pa dziko lapansi. Gawo limodzi la magawo atatu a dziko lapansi linapsa, gawo limodzi la magawo atatu a mitengo linapsa ndi gawo limodzi la magawo atatu a udzu wauwisi linapsanso.
8 Mungelo wabili wakalizya mweembo wakwe, alimwi chimwi chintu chilimbuli chiluundu chipati chiyaka mulilo chakawalilwa mulwizi.
Mngelo wachiwiri anayimba lipenga lake, ndipo chinthu china chooneka ngati phiri lalikulu loyaka moto, chinaponyedwa mʼnyanja. Gawo limodzi la magawo atatu a nyanja linasanduka magazi.
9 Chisela chatatu chazilenge zipona chakafwa achisela chatatu chabwato chakapazigwa.
Gawo limodzi mwa magawo atatu a zolengedwa zonse zamoyo za mʼnyanja, linafa, ndipo gawo limodzi la sitima za pamadzi linawonongedwa.
10 Mungelo watatu wakalizya mweembo wakwe, alimwi nyenyeezi mpati yakawa kuzwa kujulu, kibayima mbuli lampi, kuchisela chatatu chamilonga ameenda amutusawu.
Mngelo wachitatu anayimba lipenga lake, ndipo nyenyezi yayikulu, yoyaka ngati muni inachoka kumwamba nigwera pa gawo limodzi la magawo atatu a mitsinje ndi pa akasupe amadzi.
11 Izina lyanyenyezi eyo litegwa chisamu chikasala. Chisela chatatu chameenda chakaba chisamu chikasala, abantu bingi bakazwa bakajigwa ameenda alweela.
Dzina la nyenyeziyo ndi Chowawa. Gawo limodzi la magawo atatu a madzi anasanduka owawa ndipo anthu ambiri anafa chifukwa cha madzi owawawo.
12 Mungelo wane wakalizya mweembo wakwe, alimwi chisela chatatuchazuba chakawumvwa, mbuli chisela chatatu chamweezi achisela chatatu chanyenyezi. Chisela chatatu chazimwi chakasizigw, chisela chatatu chabuzuba achisela chatatu chamansiku techakachili amumuni.
Mngelo wachinayi anayimba lipenga lake, ndipo chimodzi cha zigawo zitatu za dzuwa, za mwezi ndi za nyenyezi zinamenyedwa kotero chimodzi mwa zitatu za zonsezi zinada. Panalibenso kuwala pa chimodzi mwa zigawo zitatu za usana, ndi chimodzimodzinso usiku.
13 Ndakalanga alimwi ndakamvwa chikwangala amwi malembe alabbla liti mungelomuchindi chakuti chikwangala. Oyo wakali kuluuka atata kayita ajwi pati, “' Mawe, mawe, mawe kulabo bapona anyika nkaambo kamweembo ichede yamba kulizigwa abangelo batatu.”
Ndinayangʼananso ndipo ndinaona ndi kumva chiwombankhanga chimene chinkawuluka mlengalenga kwambiri chikuyankhula mofuwula kuti, “Tsoka, Tsoka! Tsoka lalikulu kwa anthu okhala mʼdziko lapansi, angelo otsala aja akangoyimba malipenga awo!”

< Chiyubunuzyo 8 >