< Salme 63 >

1 (En salme af David, da han var i Judas ørken.) Gud, du er min Gud, dig søger jeg, efter dig tørster min Sjæl, efter dig længes mit Kød i et tørt, vansmægtende, vandløst Land
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 (således var det, jeg så dig i Helligdommen) for at skue din Vælde og Ære;
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 thi din Nåde er bedre end Liv, mine Læber skal synge din Pris.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Da vil jeg love dig hele mit Liv, opløfte Hænderne i dit Navn,
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Som med fede Retter mættes min Sjæl, med jublende Læber priser min Mund dig,
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 når jeg kommer dig i Hu på mit Leje, i Nattevagterne tænker på dig;
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 thi du er blevet min Hjælp, og jeg jubler i dine Vingers Skygge.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Dig klynger min Sjæl sig til, din højre holder mig fast.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Forgæves står de mig efter livet, i Jordens Dyb skal de synke,
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 gives i Sværdets Vold og vorde Sjakalers Bytte.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Men Kongen glædes i Gud; enhver, der sværger ved ham, skal juble, thi Løgnernes Mund skal lukkes.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Salme 63 >