< Salme 44 >

1 (Til sangmesteren. Af Koras sønner. En maskil.) Gud, vi har hørt det med egne ører, vore Fædre har fortalt os derom; du øved en Dåd i deres Dage, i Fortids Dage med din Hånd;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Folk drev du bort, men plantede hine, Folkeslag knuste du, men dem lod du brede sig;
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 thi de fik ej Landet i Eje med Sværdet, det var ej deres Arm, der gav dem Sejr, men det var din højre, din Arm og dit Ansigts Lys, thi du havde dem kær.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Du, du er min Konge, min Gud, som sender Jakob Sejr.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Ved dig nedstøder vi Fjenden, Modstanderne træder vi ned i dit Navn;
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 thi ej på min Bue stoler jeg, mit Sværd kan ikke give mig Sejr;
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 men du gav os Sejr over Fjenden, du lod vore Avindsmænd blive til Skamme.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Vi roser os altid af Gud, dit Navn vil vi love for evigt. (Sela)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Dog har du forstødt os, gjort os til Spot, du drager ej med vore Hære;
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 du lader os vige for Fjenden, vore Avindsmænd tager sig Bytte;
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 du har givet os hen som Slagtekvæg, og strøet os ud mellem Folkene,
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 dit Folk har du solgt til Spotpris, vandt ikke Rigdom ved Salget.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Til Hån for Naboer gør du os, til Spot og Spe for Grander,
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 du gør os til Mundheld blandt Folkene, lader Folkeslagene ryste på Hovedet ad os.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Min Skændsel er mig altid i Tanke, og Skam bedækker mit Åsyn
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 for spottende, hånende Tale, for Fjendens og den hævngerriges Blikke.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Alt det kom over os, skønt vi glemte dig ikke, sveg ikke heller din Pagt!
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Vort Hjerte veg ikke fra dig, vore Skridt forlod ej din Vej.
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Dog knuste du os, hvor Sjakalerne bor, og indhylled os i Mørke.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Havde vi glemt vor Guds Navn, bredt Hænderne ud mod en fremmed Gud,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 vilde Gud ej opspore det? Han kender jo Hjerternes Løn dom
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 nej, for din Skyld dræbes vi Dagen lang og regnes som Slagtekvæg!
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Vågn op, hvi sover du, Herre? Bliv vågen, forstød ej for stedse!
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Hvorfor vil du skjule dit Åsyn, glemme vor Nød og Trængsel?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Thi vor Sjæl ligger bøjet i Støvet, vort Legeme klæber ved Jorden.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Stå op og kom os til Hjælp, forløs os for din Miskundheds Skyld!
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Salme 44 >