< Salme 16 >

1 (En miktam af David.) Vogt mig, Gud, thi jeg lider på dig!
Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
2 Jeg siger til HERREN: "Du er min Herre; jeg har ikke andet Gode end dig.
Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
3 De hellige, som er i Landet, de er de herlige, hvem al min Hu står til."
Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
4 Mange Kvaler rammer dem, som vælger en anden Gud; deres Blodofre vil jeg ikke udgyde, ej tage deres Navn i min Mund.
Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
5 HERREN er min tilmålte Del og mit Bæger. Du holder min Arvelod i Hævd.
Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
6 Snorene faldt mig på liflige Steder, ja, en dejlig Arvelod tilfaldt mig.
Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
7 Jeg vil prise HERREN, der gav mig Råd, mine Nyrer maner mig, selv om Natten.
Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
8 Jeg har altid HERREN for Øje, han er ved min højre, jeg rokkes ikke.
Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
9 Derfor glædes mit Hjerte, min Ære jubler, endogså mit Kød skal bo i Tryghed.
Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 Thi Dødsriget giver du ikke min Sjæl, lader ikke din hellige skue Graven. (Sheol h7585)
chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol h7585)
11 Du lærer mig Livets Vej; man mættes af Glæde for dit Åsyn, Livsalighed er i din højre for evigt.
Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.

< Salme 16 >