< Ordsprogene 29 >

1 Hvo Nakken gør stiv, skønt revset tit, han knuses brat uden Lægedom.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Er der mange retfærdige, glædes Folket, men råder de gudløse, sukker Folket.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 Hvo Visdom elsker, glæder sin Fader, hvo Skøger omgås, bortødsler Gods.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 Kongen grundfæster Landet med Ret, en Udsuger lægger det øde.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 Mand, der smigrer sin Næste, breder et Net for hans Fod.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 I sin Brøde hildes den onde, den retfærdige jubler af Glæde.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Den retfærdige kender de ringes Retssag; den gudløse skønner intet.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Spottere ophidser Byen, men Vismænd, de stiller Vrede.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 Går Vismand i Rette med Dåre, vredes og ler han, alt preller af.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 De blodtørstige hader lydefri Mand, de retsindige tager sig af ham.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 En Tåbe slipper al sin Voldsomhed løs, Vismand stiller den omsider.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 En Fyrste, som lytter til Løgnetale, får lufter gudløse Tjenere.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Fattigmand og Blodsuger mødes, HERREN giver begges Øjne Glans.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 En Konge, der dømmer de ringe med Ret, hans Trone står fast evindelig.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 Ris og Revselse, det giver Visdom, uvorn Dreng gør sin Moder Skam.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Bliver mange gudløse tiltager Synd; retfærdige ser med Fryd deres Fald.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Tugt din Søn, så kvæger han dig og bringer din Sjæl, hvad der smager.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Uden Syner forvildes et Folk; salig den, der vogter på Loven.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 Med Ord lader Træl sig ikke tugte, han fatter dem vel, men adlyder ikke.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Ser du en Mand, der er hastig til Tale, for en Tåbe er der snarere Håb end for ham.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Forvænner man sin Træl fra ung, vil han til sidst være Herre.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 Hidsig Mand vækker Strid, vredladen Mand gør megen Synd.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Et Menneskes Hovmod ydmyger ham, den ydmyge opnår Ære.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Hæleren hader sit Liv, han hører Forbandelsen, men melder intet.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 Frygt for Mennesker leder i Snare, men den, der stoler på HERREN, er bjærget.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Mange søger en Fyrstes Gunst; Mands Ret er dog fra HERREN.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 Urettens Mand er retfærdiges Gru, hvo redeligt vandrer, gudløses Gru.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.

< Ordsprogene 29 >