< Ordsprogene 26 >

1 Som Sne om Somren og Regn Høsten så lidt hører Ære sig til for en Tåbe.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 Som en Spurv i Fart, som en Svale i Flugt så rammer ej Banden mod sagesløs Mand.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Svøbe for Hest, Bidsel for Æsel og Ris for Tåbers Ryg.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Svar ej Tåben efter hans Dårskab, at ikke du selv skal blive som han.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Svar Tåben efter hans Dårskab, at han ikke skal tykkes sig viis.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Den afhugger Fødderne og inddrikker Vold, som sender Bud ved en Tåbe.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Slappe som den lammes Ben er Ordsprog i Tåbers Mund.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Som en, der binder Stenen fast i Slyngen, er den, der hædrer en Tåbe.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Som en Tornekæp, der falder den drukne i Hænde, er Ordsprog i Tåbers Mund.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 Som en Skytte, der sårer enhver, som kommer, er den, der lejer en Tåbe og en drukken.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 Som en Hund, der vender sig om til sit Spy, er en Tåbe, der gentager Dårskab.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Ser du en Mand, der tykkes sig viis, for en Tåbe er der mere Håb end for ham.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 Den lade siger: "Et Rovdyr på Vejen, en Løve ude på Torvene!"
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 Døren drejer sig på sit Hængsel, den lade på sit Leje.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 Den lade rækker til Fadet, men gider ikke føre Hånden til Munden.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 Den lade tykkes sig større Vismand end syv, der har kloge Svar.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Den griber en Hund i Øret, som blander sig i uvedkommende Strid.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 Som en vanvittig Mand, der udslynger Gløder, Pile og Død,
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 er den, der sviger sin Næste og siger: "Jeg spøger jo kun."
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Er der intet Brænde, går Ilden ud, er der ingen Bagtaler, stilles Trætte.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 Trækul til Gløder og Brænde til Ild og trættekær Mand til at optænde Kiv.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 Bagtalerens Ord er som Lækkerbidskener, de synker dybt i Legemets Kamre.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Som Sølvovertræk på et Lerkar er ondsindet Hjerte bag glatte Læber.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 Avindsmand hykler med Læben, i sit Indre huser han Svig;
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 gør han Røsten venlig, tro ham dog ikke, thi i hans Hjerte er syvfold Gru.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Den, der dølger sit Had med Svig, hans Ondskab kommer frem i Folkets Forsamling.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 I Graven, man graver, falder man selv, af Stenen, man vælter, rammes man selv.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 Løgnetunge giver mange Hug, hyklersk Mund volder Fald.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Ordsprogene 26 >