< Ordsprogene 16 >

1 Hjertets Råd er Menneskets sag. Tungens Svar er fra HERREN.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 En Mand holder al sin Færd for ren, men HERREN vejer Ånder.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Vælt dine Gerninger på HERREN, så skal dine Planer lykkes.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Alt skabte HERREN, hvert til sit, den gudløse også for Ulykkens Dag.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Hver hovmodig er HERREN en Gru, visselig slipper han ikke for Straf.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Ved Mildhed og Troskab sones Brøde, ved HERRENs Frygt undviger man ondt.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Når HERREN har Behag i et Menneskes Veje, gør han endog hans Fjender til Venner.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Bedre er lidet med Retfærd end megen Vinding med Uret.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Menneskets Hjerte udtænker hans Vej, men HERREN styrer hans Fjed.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Der er Gudsdom på Kongens Læber, ej fejler hans Mund, når han dømmer.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Ret Bismer og Vægtskål er HERRENs, hans Værk er alle Posens Lodder.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Gudløs Færd er Konger en Gru, thi ved Retfærd grundfæstes Tronen.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Retfærdige Læber har Kongens Yndest, han elsker den, der taler oprigtigt.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Kongens Vrede er Dødens Bud, Vismand evner at mildne den.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 I Kongens Åsyns Lys er der Liv, som Vårregnens Sky er hans Yndest.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 At vinde Visdom er bedre end Guld, at vinde Indsigt mere end Sølv.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 De retsindiges Vej er at vige fra ondt; den vogter sit Liv, som agter på sin Vej.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Hovmod går forud for Fald, Overmod forud for Snublen.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Hellere sagtmodig med ydmyge end dele Bytte med stolte.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Vel går det den, der mærker sig Ordet; lykkelig den, der stoler på HERREN.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Den vise kaldes forstandig, Læbernes Sødme øger Viden.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Kløgt er sin Mand en Livsens Kilde, Dårskab er Dårers Tugt.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Den vises Hjerte giver Munden Kløgt, på Læberne lægger det øget Viden.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Hulde Ord er som flydende Honning, søde for Sjælen og sunde for Legemet.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Mangen Vej synes Manden ret, og så er dens Ende dog Dødens Veje.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 En Arbejders Hunger arbejder for ham, thi Mundens Krav driver på ham.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 En Nidding graver Ulykkesgrave, det er, som brændte der Ild på hans Læber.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 Rænkefuld Mand sætter Splid; den, der bagtaler, skiller Venner.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 Voldsmand lokker sin Næste og fører ham en Vej, der ikke er god.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Den, der stirrer, har Rænker for; knibes Læberne sammen, har man fuldbyrdet ondt.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Grå Hår er en dejlig Krone, den vindes på Retfærds Vej.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Større end Helt er sindig Mand, større at styre sit Sind end at tage en Stad.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 I Brystfolden rystes Loddet, det falder, som HERREN vil.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Ordsprogene 16 >