< 4 Mosebog 5 >

1 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Byd Israeliterne at fjerne alle spedalske fra Lejren, alle, der lider af Flåd, og alle, der er blevet urene ved Lig;
“Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
3 både Mænd og Kvinder skal I fjerne og føre uden for Lejren, for at de ikke skal gøre deres Lejr uren, hvor jeg bor midt iblandt dem.
Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
4 Det gjorde Israeliterne så; de førte dem uden for Lejren, således som HERREN havde pålagt Moses.
Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
5 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anati kwa Mose,
6 Sig til Israeliterne: Når en Mand eller Kvinde begår nogen af alle de Synder, som Mennesker begår, således at han gør sig skyldig i Svig mod HERREN, og det Menneske derved pådrager sig Skyld,
“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
7 så skal de bekende Synden, de har begået, og Gerningsmanden skal erstatte det, han har forbrudt sig med, efter dets fulde Værdi med Tillæg af en Femtedel og give det til den, han har forbrudt sig imod.
ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
8 Og hvis denne ikke har efterladt sig nogen Løser, hvem han kan yde Erstatningen, så skal Erstatningen, som ydes, tilfalde HERREN, det vil sige Præsten, foruden den Soningsvæder, ved hvilken der skaffes ham Soning.
Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
9 Al Offerydelse, alle Helliggaver, som Israeliterne frembærer til Præsten, skal tilfalde ham.
Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
10 Alle Helliggaver skal tilfalde ham; hvad nogen giver Præsten, skal tilfalde ham.
Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
11 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
12 Tal til Israeliterne og sig til dem: Når en Hustru forser sig imod sin Mand og er ham utro,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
13 idet en anden Mand har Samleje med hende, uden at det er kommet til hendes Mands Kundskab, og uden at det er blevet opdaget, skønt hun har besmittet sig, og uden at der er noget Vidne imod hende, da hun ikke er grebet på fersk Gerning,
nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
14 og han gribes af Skinsygens Ånd, så han bliver skinsyg på sin Hustru, som også i Virkeligheden har besmittet sig, eller han gribes af Skinsygens Ånd, så han bliver skinsyg på sin Hustru, skønt hun ikke har besmittet sig,
mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
15 så skal Manden bringe sin Hustru til Præsten og medbringe som Offergave for hende en Tiendedel Efa Bygmel; han må hverken hælde Olie over eller komme Røgelse på, thi det er et Skinsyge Afgrødeoffer, et Minde Afgrødeoffer, der skal minde om Brøde.
apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
16 Så skal Præsten føre hende frem og stille hende for HERRENs Åsyn.
“‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
17 Og Præsten skal tage helligt Vand i et Lerkar, og af Støvet på Boligens Gulv skal Præsten tage noget og komme i Vandet.
Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
18 Så skal Præsten stille Kvinden frem for HERRENs Åsyn, løse hendes Hår og lægge Minde Afgrødeofferet i hendes Hænder; det er et Skinsyge Afgrødeoffer; og Præsten skal have den bitre Vandes Forbandelsesvand i Hånden.
Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
19 Derpå skal Præsten besværge Kvinden og sige til hende: "Hvis ingen har haft Samleje med dig, hvis du ikke har forset dig imod din Mand og besmittet dig, så skal dette den bitre Vandes Forbandelsesvand ikke skade dig.
Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
20 Men har du forset dig imod din Mand og besmittet dig, og har en anden end din Mand haft Samleje med dig"
Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
21 Præsten besværger nu kvinden med Forbandelsens Ed og siger til hende "så gøre HERREN dig til en Forbandelse og Besværgelse i dit Folk, idet han lader din Lænd visne og din Bug svulme op;
pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
22 Forbandelsesvandet her komme ind i dine Indvolde, så din Bug svulmer op og din Lænd visner!" Og kvinden skal sige: "Amen, Amen!"
Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
23 Derpå skal Præsten skrive disse Forbandelser op på et Blad og vaske dem ud i den bitre Vandes Vand
“‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
24 og give Kvinden den bitre Vandes Forbandelsesvand at drikke, for at Forbandelsesvandet kan komme ind i hende til bitter Vånde.
Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
25 Derefter skal Præsten tage Skinsyge Afgrødeofferet af Kvindens Hånd, udføre Svingningen dermed for HERRENs Åsyn og bære det hen til Alteret.
Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
26 Og Præsten skal tage en Håndfuld af Afgrødeofferet, det, som skal ofres deraf, og bringe det som Røgoffer på Alteret og derpå give Kvinden Vandet at drikke.
Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
27 Når han har givet hende Vandet at drikke, vil Forbandelsesvandet, dersom hun har besmittet sig og været sin Mand utro, blive til bitter Vånde, når det kommer ind i hende, hendes Bug vil svulme op og hendes Lænd visne, og Kvinden bliver en Forbandelse i sit Folk.
Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
28 Men dersom Kvinden ikke har besmittet sig, dersom hun er ren, bliver hun uskadt og kan få Børn.
Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
29 Det er Loven om Skinsyge; når en Hustru forser sig imod sin Mand og besmittes,
“‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
30 eller når en Mand gribes af Skinsygens Ånd og bliver skinsyg på sin Hustru, så skal han fremstille Hustruen for HERRENs Åsyn, og Præsten skal handle med hende efter alt i denne Lov;
kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
31 Manden skal være sagesløs, men sådan en Hustru skal undgælde for sin Brøde.
Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”

< 4 Mosebog 5 >