< 4 Mosebog 2 >

1 HERREN talede til Moses og, Aron og sagde:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Israeslitene skal lejre sig hver under sit Felttegn, under sit Fædrene hus's Mærke; i en Kreds om Åbenbaringsteltet skal de lejre sig.
“Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
3 På Forsiden mod Øst skal Juda lejre sig under sin Lejrs Felttegn, Hærafdeling for Hærafdeling, med Nahasjon, Amminadabs Søn, som Øverste over Judæerne;
Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
4 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 74600 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
5 Ved Siden af ham skal Issakars Stamme lejre sig med Netanel, Zuars Søn, som Øverste over Issakariterne;
Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
6 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 54 400 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
7 Dernæst Zebulons Stamme med Eliab, Helons Søn, som Øverste over Zebuloniterne;
Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
8 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 57 400 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
9 De mønstrede i Judas Lejr udgør i alt 186 400 Mand, Hærafdeling for Hærafdeling. De skal bryde op først.
Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
10 Ruben skal lejre sig under sin Lejrs Felttegn mod Syd, Hærafdeling for Hærafdeling, med Elizur, Sjedeurs Søn, som Øverste over Rubeniterne;
Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
11 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 46 500 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
12 Ved Siden af ham skal Simeons Stamme lejre sig med Sjelumiel, Zurisjaddajs Søn, som Øverste over Simeoniterne;
Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
13 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 59300 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
14 Dernæst Gads Stamme med Eljasaf, Reuels Søn, som Øverste over Gadiferne;
Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
15 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 45 650 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
16 De mønstrede i Rubens Lejr udgør i alt 151 450 Mand, Hærafdeling for Hærafdeling. De skal bryde op i anden Række.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
17 Derpå skal Åbenbaringsteltet, Leviternes Lejr, bryde op midt imellem de andre Lejre; i den Rækkefølge, de lejrer sig, skal de bryde op, hver på sin Plads, Felttegn for Felttegn.
Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
18 Efraim skal lejre sig under sin Lejrs Felttegn mod Vest med Elisjama, Ammihuds Søn, som Øverste over Efraimiterne;
Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
19 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 40 500 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
20 Ved Siden af ham skal Manasses Stamme lejre sig med Gamliel, Pedazurs Søn, som Øverste over Manassiterne;
Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
21 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 32 200 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
22 Dernæst Benjamins Stamme med Abidan, Gidonis Søn, som Øverste over Benjaminiterne;
Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
23 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 35 400 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
24 De mønstrede i Efraims Lejr udgør i alt 108 100 Mand, Hærafdeling for Hærafdeling. De skal bryde op i tredje Række.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
25 Dan skal lejre sig under sin Lejrs Felttegn mod Nord, Hærafdeling for Hærafdeling, med Ahiezer, Ammisjaddajs Søn, som Øverste over Daniterne;
Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 62 700 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
27 Ved Siden af ham skal Asers Stamme lejre sig med Pagiel, Okrans Søn, som Øverste over Aseriterne;
Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
28 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 41 500 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
29 Dernæst Naftalis Stamme med Ahira, Enans Søn, som Øverste over Naftaliterne;
Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
30 de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op fil 53 400 Mand.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
31 De mønstrede i Dans Lejr udgør i alt 157600 Mand. De skal bryde op sidst, Felttegn for Felttegn.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
32 Det var de mønstrede af Israeliterne efter deres Fædrenehuse, alle de mønstrede i Lejrene, Hærafdeling for Hærafdeling, 603 550 Mand.
Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
33 Men Leviterne mønstredes ikke sammen med de andre Israelitter, således som HERREN havde pålagt Moses.
Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
34 Og ganske som HERREN havde pålagt Moses, slog Israeliterne Lejr, Felttegn for Felttegn, og i den Rækkefølge brød de op, enhver med sine Slægter, med sit Fædrenehus.
Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.

< 4 Mosebog 2 >