< Nehemias 2 >

1 I Nisan Måned i Kong Artaxerxes's tyvende Regeringsår, da jeg skulde sørge for Vin, har jeg engang Vinen frem og rakte Kongen den. Jeg havde ikke før set modfalden ud, når jeg stod for hans Ansigt.
Pa mwezi wa Nisani, mʼchaka cha makumi awiri cha ufumu wa Aritasasita, atabwera ndi vinyo pamaso pa mfumu ine ndinatenga vinyoyo ndi kupereka kwa mfumu. Koma ndinali ndisanakhalepo ndi nkhope yachisoni pamaso pake.
2 Og Kongen sagde til mig: Hvorfor ser du så modfalden ud? Du er jo ikke syg; det kan ikke være andet, end at du har en Hjertesorg! Da blev jeg såre bange,
Tsono mfumu inandifunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani nkhope yako ikuoneka yachisoni pamene iwe sukudwala? Ichi si chinthu china koma chisoni cha mu mtima.” Ine ndinachita mantha kwambiri.
3 og jeg sagde til Kongen: "Kongen leve evindelig! Hvor kan jeg andet end se modfalden ud, når den By, hvor mine Fædres Grave er, ligger øde, og dens Porte er fortæret af Ilden?
Ndinawuza mfumu kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wamuyaya! Kodi nkhope yanga ilekerenji kuoneka yachisoni pamene mzinda umene kuli manda a makolo anga, wasanduka bwinja ndipo zipata zake zinawonongedwa ndi moto?”
4 Kongen spurgte mig da: "Hvad er det, du ønsker? Så bad jeg til Himmelens Gud,"
Apo mfumu inandifunsa kuti, “Tsono ukufuna kundipempha chiyani?” Ndipo ine ndinapemphera kwa Mulungu Wakumwamba.
5 og jeg sagde til Kongen: "Hvis Kongen synes, og hvis din Tjener er dig til Behag, beder jeg om, at du vil lade mig rejse til Juda, til den By, hvor mine Fædres Grave er, og lade mig bygge den op igen!
Ndipo ndinayankha kuti, “Ngati amfumu chingakukondweretseni, ngati mungakomere mtima mtumiki wanune, mundilole kuti ndipite ku Yuda, ku mzinda kumene kuli manda a makolo anga kuti ndikawumangenso.”
6 Da sagde Kongen til mig, medens Dronningen sad ved hans Side: "Hvor længe vil den Rejse vare, og hvornår kan du vende tilbage? Og da Kongen således fandt for godt at lade mig rejse, opgav jeg ham en Tid.
Tsono mfumu, mfumukazi itakhala pambali pake, anandifunsa kuti, “Kodi kumeneko ukakhalako masiku angati ndipo udzabwera liti?” Ndinayiwuza mfumu nthawi yake ndipo inandilola kuti ndipite.
7 Og jeg sagde til Kongen: Hvis Kongen synes, så lad mig få Breve med til Statholderne hinsides Floden, så de lader mig drage videre, til jeg når Juda,
Ndipo ndinatinso kwa mfumu, “Ngati zikondweretse mfumu, mundipatse makalata oti ndikapereke kwa abwanamkubwa a ku chigawo cha Patsidya pa Yufurate, kuti akandilole kudutsa mwamtendere mpaka nditakafika ku Yuda.
8 og et Brev til Asaf, Opsynsmanden. over den kongelige Skov, at han skal give mig Træ til Bjælkeværket i Tempelborgens Porte og til Byens Mur og det Hus, jeg tager ind i! Det gav Kongen mig, eftersom min Guds gode Hånd var over mig.
Mundipatsenso kalata yokapereka kwa Asafu woyangʼanira nkhalango ya mfumu, kuti akandipatse mitengo yokapangira mitanda ya zipata za nsanja yoteteza Nyumba ya Mulungu, mitanda ya khoma la mzinda ndi ya nyumba yokhalamo ine.” Mfumu indipatse zomwe ndinapempha popeza Yehova wokoma mtima anali nane.
9 Da jeg kom til Statholderne hinsides Floden, gav jeg dem Kongens Breve; desuden havde Kongen givet mig Hærførere og Ryttere med på Rejsen.
Choncho ndinanyamuka ulendo wanga ndipo ndinafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Mfumu nʼkuti itatumiza akulu ankhondo ndi okwera pa akavalo kuti atsagane nane.
10 Men da Horoniten Sanballat og den ammonitiske Træl Tobija hørte det, ærgrede de sig højligen over, at der var kommet en Mand for at arbejde på Israeliternes Bedste.
Sanibalati wa ku Horoni ndi Tobiya wa ku Amoni atamva zimenezi, iwo anayipidwa kwambiri kuti wina wabwera kudzachitira zabwino Aisraeli.
11 Så kom jeg til Jerusalem, og da jeg havde været der i tre Dage,
Ndinafika ku Yerusalemu, ndipo ndinakhala kumeneko masiku atatu.
12 brød jeg op ved Nattetide sammen med nogle få Mænd uden at have sagt noget Menneske, hvad min Gud havde skudt mig i Sinde at gøre for Jerusalem; og der var intet andet Dyr med end det, jeg red på.
Sindinawuze munthu aliyense za zimene Yehova anayika mu mtima mwanga kuti ndichitire mzinda wa Yerusalemu. Choncho ndinanyamuka usiku pamodzi ndi anthu ena owerengeka. Ndinalibe bulu wina aliyense kupatula amene ndinakwerapo.
13 Jeg red så om Natten ud gennem Dalporten i Retning af Dragekilden og hen til Møgporten, idet jeg undersøgte Jerusalems Mure, der var nedrevet, og Portene, der var fortæret af Ilden;
Ndinatuluka usiku podzera ku Chipata cha ku Chigwa ndi kuyenda kupita ku Chitsime cha Chirombo Chamʼmadzi mpaka ku Chipata cha Zinyalala. Ndinayangʼana makoma a Yerusalemu, amene anagwetsedwa, ndi zipata zake, zimene zinawonongedwa ndi moto.
14 derpå red jeg videre til Kildeporten og Kongedammen, men der var ikke Plads nok til, at mit Ridedyr kunde komme frem med mig.
Kenaka ndinapita ku Chipata cha Kasupe ndi ku Dziwe la Mfumu. Koma panalibe malo okwanira akuti bulu wanga adutse.
15 Så red jeg om Natten op igennem Dalen og undersøgte Muren, forandrede Retning og red så ind igennem Dalporten, hvorpå jeg vendte hjem.
Kotero usikuwo ndinapita ku chigwa, ndikuyangʼana khomalo. Pomaliza ndinabwerera ndi kukalowanso mu mzinda kudzera ku Chipata cha ku Chigwa.
16 Forstanderne vidste ikke, hvor jeg var gået hen, eller hvad jeg foretog mig; og hverken Jøderne, Præsterne, Stormændene, Forstanderne eller de andre, der skulde have med Arbejdet at gøre, havde jeg endnu sagt noget.
Akuluakulu sanadziwe kumene ndinapita kapena zimene ndimachita, chifukwa pa nthawiyi nʼkuti ndisananene kalikonse kwa Ayuda kapena ansembe, anthu olemekezeka kapena akuluakulu, kapena wina aliyense amene anali woyenera kugwira ntchitoyi.
17 Men nu sagde jeg til dem: I ser den Ulykke, vi er i, hvorledes Jerusalem er ødelagt og Portene opbrændt; kom derforog lad os opbygge Jerusalems Mur, så vi ikke mere skal være til Spot!
Ndinawawuza kuti, “Inu mukuona mavuto amene tili nawo. Mukuona kuti mzinda wa Yerusalemu wasanduka bwinja ndipo zipata zake zatenthedwa ndi moto. Tsono tiyeni timangenso makoma a Yerusalemu ndipo sitidzachitanso manyazi.”
18 Og da jeg fortalte dem, hvorledes min Guds gode Hånd havde været over mig, og om de Ord, Kongen havde talt til mig, sagde de: Lad os gøre os rede og bygge! Og de tog sig sammen til det gode Værk.
Ndinawawuza za mmene Yehova Mulungu wanga anandichitira zabwino ndiponso mawu amene mfumu inandiwuza. Tsono anati, “Tiyeni tiyambenso kumanga.” Kotero analimbitsana mtima kuti ayambenso ntchito yabwinoyi.
19 Da Horoniten Sanballat, den ammonitiske Træl Tobija og Araberen Gesjem hørte det, spottede de os og sagde hånligt til os: Hvad er det, I der har for? Sætter I eder op mod Kongen?
Koma Sanibalati wa ku Horoni, Tobiya wa ku Amoni ndi Gesemu Mwarabu atamva zimenezi, anatiseka ndi kutinyoza. Iwo anafunsa kuti, “Kodi muti ndi chiyani chimene mukuchitachi? Kodi mufuna kuwukira mfumu?”
20 Men jeg gav dem til Svar: "Himmelens Gud vil lade det lykkes for os, og vi, hans Tjenere, vil gøre os rede og bygge; men I har ingen Del eller Ret eller Ihukommelse i Jerusalem!"
Koma ndinawayankha kuti, “Mulungu Wakumwamba atithandiza kuti zinthu zitiyendere bwino. Ife antchito ake tiyambapo kumanga. Koma inu mulibe gawo lanu muno mu Yerusalemu. Mulibe chokuyenerezani kulandira malo ano. Mulibenso chilichonse muno chokumbutsa za inu.”

< Nehemias 2 >