< Lukas 21 >

1 Men idet han så op, fik han Øje på de rige, som lagde deres Gaver i Tempelblokken.
Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
2 Men han så en fattig Enke. som lagde to Skærve deri.
Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
3 Og han sagde: "Sandelig, siger jeg eder, at denne fattige Enke lagde mere i end de alle.
Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
4 Thi alle disse lagde af deres Overflod hen til Gaverne; men hun lagde af sin Fattigdom al sin Ejendom, som hun havde."
Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
5 Og da nogle sagde om Helligdommen, at den var prydet med smukke Sten og Tempelgaver. sagde han:
Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
6 "Disse Ting, som I se - der skal komme Dage, da der ikke lades Sten på Sten, som jo skal nedbrydes."
“Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
7 Men de spurgte ham og sagde: "Mester! når skal dette da ske? og hvad er Tegnet på, når dette skal ske?"
Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
8 Men han sagde: "Ser til, at I ikke blive forførte; thi mange skulle på mit Navn komme og sige: Det er mig, og: Tiden er kommen nær. Går ikke efter dem!
Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
9 Men når I høre om Krige og Oprør, da forskrækkes ikke; thi dette må først ske, men Enden er der ikke straks."
Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
10 Da sagde han til dem: "Folk skal rejse sig imod Folk, og Rige imod Rige.
Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
11 Og store Jordskælv skal der være her og der og Hungersnød og Pest, og der skal ske frygtelige Ting og store Tegn fra Himmelen.
Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
12 Men forud for alt dette skulle de lægge Hånd på eder og forfølge eder og overgive eder til Synagoger og Fængsler, og I skulle føres frem for Konger og Landshøvdinger for mit Navns Skyld.
“Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
13 Det skal falde ud for eder til Vidnesbyrd.
Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
14 Lægger det da på Hjerte, at I ikke forud skulle overtænke, hvorledes I skulde forsvare eder.
Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
15 Thi jeg, vil give eder Mund og Visdom, som alle eders Modstandere ikke skulle kunne modstå eller modsige.
Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
16 Men I skulle endog forrådes af Forældre og Brødre og Frænder og Venner, og de skulle slå nogle af eder ihjel.
Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
17 Og I skulle hades af alle for mit Navns Skyld.
Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
18 Og ikke et Hår på eders Hoved skal gå tabt.
Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
19 Ved eders Udholdenhed skulle I vinde eders Sjæle.
Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
20 Men når I se Jerusalem omringet af Krigshære, da forstår, at dens Ødelæggelse er kommen nær.
“Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
21 Da skulle de, som ere i Judæa, fly til Bjergene; og de, som ere inde i Staden, skulle vige bort derfra; og de, som ere på Landet, skulle ikke gå ind i den.
Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
22 Thi disse ere Hævnens Dage, da alt, hvad skrevet er, skal opfyldes.
Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
23 Men ve de frugtsommelige og dem, som give Die, i de Dage; thi der skal være stor Nød på Jorden og Vrede over dette Folk.
Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
24 Og de skulle falde for Sværdets Od og føres fangne til alle Hedningerne; og Jerusalem skal nedtrædes af Hedningerne, indtil Hedningernes Tider fuldkommes.
Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
25 Og der skal ske Tegn i Sol og Måne og Stjerner, og på Jorden skulle Folkene ængstes i Fortvivlelse over Havets og Bølgernes Brusen,
“Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
26 medens Mennesker forsmægte af Frygt og Forventning om de Ting, som komme over Jorderige; thi Himmelens Kræfter skulle rystes.
Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
27 Og da skulle de se Menneskesønnen komme i Sky med Kraft og megen Herlighed.
Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
28 Men når disse Ting begynde at ske, da ser op og opløfter eders Hoveder, efterdi eders Forløsning stunder til."
Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
29 Og han sagde dem en Lignelse: "Ser Figentræet og alle Træerne;
Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
30 når de alt springe ud, da se I og skønne af eder selv, at Sommeren nu er nær.
Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
31 Således skulle også I, når I se disse Ting ske, skønne, at Guds Rige er nær.
Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
32 Sandelig, siger jeg eder, at denne Slægt skal ingenlunde forgå, førend det er sket alt sammen.
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
33 Himmelen og Jorden skulle forgå; men mine Ord skulle ingenlunde forgå.
Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
34 Men vogter eder, at eders Hjerter ikke, nogen Tid besværes af Svir og Drukkenskab og timelige Bekymringer, så hin dag kommer pludseligt over eder som en Snare.
“Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
35 Thi komme skal den over alle dem, der bo på hele Jordens Flade.
Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
36 Og våger og beder til enhver Tid, for at I må blive i Stand til at undfly alle disse Ting, som skulle ske, og bestå for Menneskesønnen."
Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
37 Men han lærte om Dagene i Helligdommen, men om Nætterne gik han ud og overnattede på det Bjerg, som kaldes Oliebjerget.
Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
38 Og hele Folket kom årle til ham i Helligdommen for at høre ham.
Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.

< Lukas 21 >