< Dommer 21 >

1 Men Israels Mænd havde i Mizpa aflagt den Ed: "Ingen af os vil give en Benjaminit sin Datter til Ægte!"
Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
2 Da nu Folket var kommet til Betel, sad de der lige til Aften for Guds Åsyn og opløftede deres Røst, græd heftigt
Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
3 og sagde: "Hvorfor, HERRE, Israels Gud, er dog dette hændet i Israel, så at vi i Dag må savne en Stamme af Israel?"
Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
4 Tidligt næste Morgen byggede Folket et Alter der og ofrede Brændofre og Takofre.
Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
5 Derpå sagde Israelitterne: "Hvem blandt alle Israels Stammer undlod at drage op med Forsamlingen til HERREN?" Der var nemlig svoret en dyr Ed på, at enhver, der undlod at drage op til HERREN i Mizpa, skulde dø.
Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
6 Men nu gjorde det Israelitterne ondt for deres Broder Benjamin, og de sagde: "I Dag er en Stamme hugget af Israel!
Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
7 Hvad skal vi gøre for dem, der er tilbage, for at skaffe dem Hustruer, eftersom vi har svoret ved HERREN, at vi ikke vil give dem nogen af vore Døtre fil Ægte?"
Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
8 Så spurgte de: "Er der måske en af Israels Stammer, der undlod at drage op til HERREN i Mizpa?" Og se, der var ingen kommet til Lejren, til Forsamlingen, fra Jabesj i Gilead.
Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
9 Så blev Folket mønstret, og se, der var ingen af Indbyggerne fra Jabesj i Gilead.
Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
10 Da sendte Menigheden 12000 Mand af de tapreste Folk derhen med den Befaling: "Drag hen og hug Indbyggerne i Jabesj i Gilead ned med Sværdet tillige med deres Kvinder og Børn.
Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
11 Således skal I bære eder ad: Alle af Mandkøn og alle Kvinder, der har haft Omgang med Mænd, skal I lægge Band på!"
Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
12 De fandt så hos Indbyggerne i Jabesj i Gilead 400 unge Piger, der var Jomfruer og ikke havde haft Omgang med nogen Mand, og dem førte de til Lejren i Silo i Kana'ans Land.
Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
13 Derpå sendte hele Menigheden Sendebud hen for af underhandle med Benjaminiterne, der befandt sig på Rimmons Klippe, og tilbyde dem Fred.
Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
14 På det Tidspunkt vendte Benjaminiterne så tilbage, og de gav dem de Kvinder fra Jabesj i Gilead, som man havde ladet i Live. Men de var ikke nok til dem.
Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
15 Da gjorde det Folket ondt for Benjamin, fordi HERREN havde gjort et Skår i Israels Stammer.
Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
16 Og Menighedens Ældste sagde: "Hvad skal vi gøre for dem, der er tilbage, for at skaffe dem Hustruer, eftersom alle Kvinder i Benjamin er udryddet?"
Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
17 Og de sagde: "Hvorledes kan der reddes en Rest af Benjamin, så at ikke en Stamme i Israel går til Grunde?
Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
18 Vi kan jo ikke give dem nogen af vore Døtre til Ægte!" Israelitterne havde nemlig svoret og sagt: "Forbandet være den, som giver Benjaminiterne en Hustru!"
Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
19 Da sagde de: "Se, HERRENs Højtid fejres jo hvert År i Silo!" Det ligger norden for Betel, østen for Vejen, der fører op fra Betel til Sikem, og sønden for Lebona.
Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
20 Og de bød Benjaminiterne: "Gå hen og læg eder på Lur i Vingårdene!
Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
21 Se så nøje til, og når de unge Kvinder fra Silo kommer ud for at opføre deres Danse, skal I komme frem af Vingårdene og røve hver sin Hustru af de unge Kvinder fra Silo og så drage hjem til Benjamins Land!
ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
22 Når så deres Fædre eller Brødre kommer for at gå i Rette med eder, skal I sige til dem: Skån os, thi vi fik os ikke alle en Hustru i Krigen! Det er jo ikke eder, der har givet os dem; i så Fald vilde I have forbrudt eder!"
Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
23 Det gjorde Benjaminiterne da, og de tog sig Hustruer af de dansende Kvinder, som de røvede, een til hver; derpå vendte de tilbage til deres Arvelod, opbyggede deres Byer og boede i dem.
Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
24 Og samtidig drog Israelitterne derfra, hver til sin Stamme og Slægt, og de gik derfra hver til sin Arvelod,
Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
25 I de Dage var der ingen Konge i Israel; enhver gjorde, hvad han fandt for godt.
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.

< Dommer 21 >