< Jeremias 27 >

1 I Josiass Søns, Kong Jojakim af Judas, første regeringstid kom dette Ord til Jeremias fra HERREN:
Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Således sagde HERREN til mig: Gør dig Reb og Ågstænger og læg dem på din Hals
“Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako.
3 og send Edoms, Moabs, Ammoniternes, Tyruss og Zidons Konger Bud ved deres Sendemænd, som er kommet til Kong Zedekias af Juda i Jerusalem;
Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda.
4 byd dem at sige til deres Herrer: Så siger Hærskarers HERRE. Israels Gud: Sig til eders Herrer:
Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti:
5 Jeg skabte Jorden og Menneskene og Kvæget på Jorden ved min vældige Styrke og min udrakte Hånd, og jeg giver den, til hvem jeg finder for godt.
Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna.
6 Og nu giver jeg alle disse Lande i min Tjener Kong Nebukadnezar af Babels Hånd, selv Markens Vildt giver jeg hen til at trælle for ham.
Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire.
7 Alle Folk skal trælle for ham, hans Søn og Sønnesøn, indtil også hans Lands Time slår og mange Folkeslag og store Konger gør ham til deres Træl.
Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.
8 Og det Folk og det Rige, som ikke vil trælle for ham, Kong Nebukadnezar af Babel, og bøje Hals under Babels Konges Åg, det vil jeg hjemsøge med Sværd, Hunger og Pest, lyder det fra HERREN, til det er tilintetgjort ved hans Hånd.
“‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu.
9 I skal ikke høre på eders Profeter og Spåmænd, eders Drømmere, Sandsigere og Troldmænd, som siger til eder: "I skal ikke komme til at trælle for Babels Konge;
Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’
10 thi det er Løgn, de profeterer for eder for at få eder bort fra eders Jord, idet jeg da driver eder bort og I går til Grunde.
Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu.
11 Men det Folk, der bøjer Hals under Babels Konges Åg og træller for ham, vil jeg lade blive på sin Jord, lyder det fra HERREN, så det kan dyrke den og bo der.
Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’”
12 Og til Kong Zedekias af Juda talte jeg i Overensstemmelse med alle disse Ord: Bøj Hals under Babels Konges Åg og træl for ham og hans Folk, så skal I leve.
Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo.
13 Hvorfor vil du og dit Folk dø ved Sværd, Hunger og Pest, således som HERREN truede det Folk, der ikke vil trælle for Babels Konge?
Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni?
14 Hør ikke på Profeternes Ord, når de siger til eder: "I skal ikke komme til at trælle for Babels Konge"; thi Løgn profeterer de eder.
Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza.
15 Jeg har ikke sendt dem, lyder det fra HERREN, og de profeterer Løgn i mit Navn, for at jeg skal bortstøde eder, så I går til Grunde sammen med Profeterne, der profeterer for eder.
Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”
16 Og til Præsterne og alt dette Folk talte jeg således: Så siger HERREN: Hør ikke på eders Profeters Ord, når de profeterer for eder og siger: "Se, HERRENs Huss Kar skal nu snart føres hjem fra Babel." Thi Løgn profeterer de eder.
Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu.
17 Hør dem ikke, men træl for Babels Konge, så skal I leve. Hvorfor skal denne By lægges øde?
Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja?
18 Er de Profeter og har HERRENs Ord, så lad dem gå i forbøn hos Hærskarers HERRE, at de Kar, der er tilbage i HERRENs Hus og Judas konges Palads, ikke også skal komme til Babel.
Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni.
19 Thi så siger Hærskarers HERRE om Søjlerne, Havet og Stellene og om de sidste Kar, der er tilbage i denne By,
Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu.
20 dem, som Kong Nebukadnezar af Babel ikke tog med, da han bortførte Jojakims søn, Kong Jekonja af Juda, fra Jerusalem til Babel med alle de ypperste i Juda og Jerusalem,
Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
21 ja, så siger Hærskarers HERRE, Israels Gud, om de kar, der er tilbage i HERRENs Hus og Judas Konges Palads og i Jerusalem:
Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti,
22 De skal føres til Babel, og der skal de blive, til den Dag jeg tager mig af dem og fører dem op og bringer dem tilbage hertil, lyder det fra HERREN.
‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’”

< Jeremias 27 >