< 1 Mosebog 39 >

1 Da Josef var bragt ned til Ægypten, blev han af Ismaeliterne, der havde bragt ham derned, solgt til Faraos Hofmand Potifar, Livvagtens Øverste, en Ægypter.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 Men HERREN var med Josef, så Lykken fulgte ham. Han var i sin Herre Ægypterens Hus;
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 og hans Herre så, at HERREN var med ham, og at HERREN lod alt, hvad han foretog sig, lykkes for ham.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 Således fandt Josef Nåde for hans Øjne og kom til at gå ham til Hånde; og han satte ham over sit Hus og gav alt, hvad han ejede, i hans Hånd;
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 og fra det Øjeblik han satte ham over sit Hus og alt, hvad han ejede, velsignede HERREN Ægypterens Hus for Josefs Skyld, og HERRENs Velsignelse hvilede over alt, hvad han ejede, både inde og ude;
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 og han betroede alt, hvad han ejede, til Josef, og selv bekymrede han sig ikke om andet end den Mad, han spiste. Men Josef havde en smuk Skikkelse og så godt ud.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 Nu hændte det nogen Tid derefter, at hans Herres Hustru kastede sine Øjne på Josef og sagde: "Kom og lig hos mig!"
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 Men han vægrede sig og sagde til sin Herres Hustru: "Se, min Herre bekymrer sig ikke om noget i Huset, men alt, hvad han ejer, har han givet i min Hånd;
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 han har ikke større Magt i Huset end jeg, og han har ikke unddraget mig noget som helst undtagen dig, fordi du er hans Hustru hvor skulde jeg da kunne øve denne store Misgerning og synde mod Gud!"
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 Og skønt hun Dag efter Dag talte Josef til, vilde han dog ikke føje hende i at ligge hos hende og have med hende at gøre.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Men en Dag han kom ind i Huset for at gøre sin Gerning, og ingen af Husfolkene var til Stede i Huset,
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 greb hun fat i hans Kappe og sagde: "Kom og lig hos mig!" Men han lod Kappen blive i hendes Hånd og flygtede ud af Huset.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 Da hun nu så, at han havde ladet hende beholde Kappen og var flygtet ud af Huset,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 kaldte hun på sine Husfolk og sagde til dem: "Her kan I se! Han har bragt os en Hebræer til at drive Spot med os! Han kom ind til mig og vilde ligge hos mig, men jeg råbte af alle Kræfter,
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 og da han hørte, at jeg gav mig til at råbe, lod han sin Kappe blive hos mig og flygtede ud af Huset!"
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 Så lod hun Kappen blive liggende hos sig, indtil hans Herre kom hjem,
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 og sagde så det samme til ham: "Den hebraiske Træl, du bragte os til at drive Spot med os, kom ind til mig;
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 men da jeg gav mig til at råbe, lod han sin Kappe blive hos mig og flygtede ud af Huset."
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 Da hans Herre hørte sin Hustrus Ord: "Således har din Træl behandlet mig!" blussede Vreden op i ham;
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 og Josefs Herre tog ham og kastede ham i Fængsel der, hvor Kongens Fanger sad fængslet. Således kom Josef i Fængsel.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 Men HERREN var med Josef og skaffede ham Yndest og lod ham finde Nåde hos Fængselets Overopsynsmand,
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 så at han gav ham Opsyn over alle Fangerne i Fængselet, og han sørgede for alt, hvad der skulde gøres der.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 Fængselets Overopsynsmand førte ikke Tilsyn med noget som helst af, hvad der var lagt i Josefs Hånd, eftersom HERREN var med ham og lod alt, hvad han foretog sig, lykkes.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< 1 Mosebog 39 >