< 1 Mosebog 30 >

1 Da Rakel så, at hun ikke fødte Jakob noget Barn, blev hun skinsyg på sin Søster og sagde til Jakob: "Skaf mig Børn, ellers dør jeg!"
Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
2 Men Jakob blev vred på Rakel og sagde: "Er jeg i Guds Sted? Det er jo ham, der har nægtet dig Livsfrugt!"
Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
3 Så sagde hun: "Der er min Trælkvinde Bilha; gå ind til hende, så hun kan føde på mine Knæ og jeg få Sønner ved hende!"
Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
4 Og hun gav ham sin Trælkvinde Bilha til Hustru, og Jakob gik ind til hende.
Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
5 Så blev Bilha frugtsommelig og fødte Jakob en Søn,
ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
6 og Rakel sagde: "Gud har hjulpet mig til min Ret, han har hørt min Røst og givet mig en Søn." Derfor gav hun ham Navnet Dan.
Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
7 Siden blev Rakels Trælkvinde Bilha frugtsommelig igen og fødte Jakob en anden Søn;
Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
8 og Rakel sagde: "Gudskampe har jeg kæmpet med min Søster og sejret." Derfor gav hun ham Navnet Naftali.
Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
9 Men da Lea så, at hun ikke fik flere Børn, tog hun sin Trælkvinde Zilpa og gav Jakob hende til Hustru;
Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
10 og da Leas Trælkvinde Zilpa fødte Jakob en Søn,
Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
11 sagde Lea: "Hvilken Lykke!" Derfor gav hun ham Navnet Gad.
Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
12 Siden fødte Leas Trælkvinde Zilpa Jakob en anden Søn;
Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
13 og Lea sagde: "Held mig! Kvinderne vil prise mit Held!" Derfor gav hun ham Navnet Aser.
Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
14 Men da Ruben engang i Hvedehøstens Tid gik på Marken, fandt han nogle Kærlighedsæbler og bragte dem til sin Moder Lea. Da sagde Rakel til Lea: "Giv mig nogle af din Søns Kærlighedsæbler!"
Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
15 Lea svarede: "Er det ikke nok, at du har taget min Mand fra mig? Vil du nu også tage min Søns Kærlighedsæbler?" Men Rakel sagde: "Til Gengæld for din Søns Kærlighedsæbler må han ligge hos dig i Nat!"
Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
16 Da så Jakob kom fra Marken om Aftenen, gik Lea ham i Møde og sagde: "Kom ind til mig i Nat, thi jeg har købt dig for min Søns Kærlighedsæbler!" Og han lå hos hende den Nat.
Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
17 Så bønhørte Gud Lea, og hun blev frugtsommelig og fødte Jakob en femte Søn;
Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
18 og Lea sagde: "Gud har lønnet mig, fordi jeg gav min Mand min Trælkvinde." Derfor gav hun ham Navnet Issakar.
Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
19 Siden blev Lea frugtsommelig igen og fødte Jakob en sjette Søn;
Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
20 og Lea sagde: "Gud har givet mig en god Gave, nu vil min Mand blive hos mig, fordi jeg har født ham seks Sønner." Derfor gav hun ham Navnet Zebulon.
Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
21 Siden fødte hun en Datter, som hun gav Navnet Dina.
Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
22 Så kom Gud Rakel i Hu, og Gud bønhørte hende og åbnede hendes Moderliv,
Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
23 så hun blev frugtsommelig og fødte en Søn; og hun sagde: "Gud har borttaget min Skændsel."
Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
24 Derfor gav hun ham Navnet Josef; thi hun sagde: "HERREN give mig endnu en Søn!"
Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
25 Da Rakel havde født Josef. sagde Jakob til Laban: "Lad mig fare, at jeg kan drage til min Hjemstavn og mit Land;
Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
26 giv mig mine Hustruer og mine Børn som jeg har tjent dig for, og lad mig drage bort; du ved jo selv, hvorledes jeg har tjent dig!"
Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
27 Men Laban svarede: "Måtte jeg have fundet Nåde for dine Øjne! Jeg har udfundet, at HERREN bar velsignet mig for din Skyld."
Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
28 Og han sagde: "Bestem, hvad du vil have i Løn af mig, så vil jeg give dig den!"
Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
29 Så sagde Jakob: "Du ved jo selv, hvorledes jeg har tjent dig, og hvad din Ejendom er blevet til under mine Hænder;
Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
30 thi før jeg kom, ejede du kun lidet, men nu har du Overflod; HERREN har velsignet dig, hvor som helst jeg satte min Fod. Men når kan jeg komme til at gøre noget for mit eget Hus?"
Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
31 Laban svarede: "Hvad skal jeg da give dig?" Da sagde Jakob: "Du skal ikke give mig noget; men hvis du går ind på, hvad jeg nu foreslår dig, vedbliver jeg at være Hyrde for dine Hjorde og vogte dem.
Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
32 Jeg vil i Dag gå hele din Hjord igennem og udskille alle spættede og blakkede Dyr alle de sorte Får og de blakkede eller spættede Geder skal være min Løn;
Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
33 i Morgen den Dag skal min Retfærdighed vidne for mig: Når du kommer og syner den Hjord, der skal være min Løn, da er alle de" Geder, som ikke er spættede eller blakkede, og de Får, som ikke er sorte, stjålet af mig."
Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
34 Laban svarede: "Vel, lad det blive, som du siger!"
Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
35 Så udskilte han samme Dag de stribede og blakkede Bukke og de spættede og blakkede Geder, alle dem der havde hvide Pletter, og alle de sorte Får og overgav dem til sine Sønner,
Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
36 og han lod der være tre Dagsrejser mellem dem og Jakob; og Jakob vogtede Resten af Labans Hjord.
Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
37 Men Jakob tog friske Grene af Hvidpopler, Mandeltræer og Plataner og afskrællede Barken således, at der kom hvide Striber på Grenene;
Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
38 og de afskrællede Grene stillede han op i Trugene foran Dyrene, i Vandrenderne, hvor Dyrene kom hen og drak; og de parrede sig, når de kom for at drikke;
Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
39 Dyrene parrede sig foran Grenene og fødte så stribet, spættet og blakket Afkom.
Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
40 Og Lammene udskilte Jakob. Og han lod Dyrene vende Hovedet mod de stribede og alle de sorte dyr i Labans Hjord. På den Måde fik han sine egne Hjorde, som han ikke bragte sammen med Labans.
Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
41 Og hver Gang de kraftige Dyr parrede sig, stillede Jakob Grenene op foran dem i Vandrenderne, for at de skulde parre sig foran Grenene;
Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
42 men når det var de svage Dyr, stillede han dem ikke op; således kom de svage til at tilhøre Laban, de kraftige Jakob.
Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
43 På den Måde blev Manden overmåde rig og fik Småkvæg i Mængde, Trælkvinder og Trælle, Kameler og Æsler.
Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.

< 1 Mosebog 30 >