< Ezra 4 >

1 Men da Judas og Benjamins Fjender hørte, at de, der havde været i Landflygtighed, byggede HERREN, Israels Gud, en Helligdom,
Adani a Yuda ndi Benjamini anamva kuti anthu obwera ku ukapolo aja akumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli.
2 henvendte de sig til Zerubbabel, Jesua og Overhovederne for Fædrenehusene og sagde til dem: Lad os være med til at bygge, thi vi søger eders Gud såvel som I, og ham har vi ofret til, siden Assyrerkongen Asarhaddon førte os herhen!
Tsono anapita kwa Zerubabeli ndi kwa atsogoleri a mabanja awo ndi kunena kuti, “Mutilole kuti tikuthandizeni kumangaku chifukwa ife timapembedza Mulungu wanu monga momwe mumachitira inu, ndipo takhala tikupereka nsembe kwa Iye kuyambira nthawi ya Esrahadoni, mfumu ya ku Asiriya, amene anabwera nafe kuno.”
3 Men Zerubbabel, Jesua og de andre Overhoveder for Israels Fædrenehuse svarede: I skal ikke være fælles med os om at bygge vor Gud et Hus, men vi vil være ene om at bygge for HERREN, Israels Gud, således som Kong Kyros, Perserkongen, pålagde os!"
Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”
4 Så bragte Hedningerne i Landet Judas Folks Hænder til at synke og skræmmede dem fra at bygge;
Tsono anthu a mʼdzikomo anayamba kuchititsa ulesi anthu a ku Yuda, ndi kuwachititsa mantha kuti aleke ntchito yomangayo.
5 og de købte Folk til med deres Råd at modarbejde dem og bringe deres Planer til at strande; således gik det, så længe Perserkongen Kyros levede, lige til Perserkongen Darius's Regering.
Analemba alangizi ena kuti alepheretse cholinga chawo pa ntchitoyo pa nthawi yonse ya Koresi, mfumu ya ku Perisiya, ndiponso mpaka pamene Dariyo mfumu ya ku Perisiya ankalamulira dzikolo.
6 Under Ahasverus's Regering, i hans første Regeringstid, skrev de en Klage oer Judas og Jerusalems lodbyggere.
Mfumu Ahasiwero atangoyamba kulamulira dzikolo, adani aja analemba kalata yoneneza anthu a Yuda ndi Yerusalemu.
7 I Artaxerxes's Dage affattede Bisjlam, Mitredat, Tabe'el og alle hans andre Embedsbrødre en Skrivelse til Perserkongen Artaxerxes. Skrivelsen var affattet på Aramaisk og oversat.
Ndiponso mʼnthawi ya Aritasasita mfumu ya Perisiya, Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli ndi anzawo ena analemba kalata inanso kwa Aritasasita. Kalatayo inalembedwa mʼChiaramu ndipo ankatanthauzira poyiwerenga.
8 Statholderen Rehum og Skriveren Sjimsjaj skrev et Brev mod Jerusalem til Kong Artaxerxes af følgende Indhold.
Rehumu mkulu wankhondo ndi Simisai mlembi, nawonso analemba kalata yawo yoneneza anthu a ku Yerusalemu kwa mfumu Aritasasita. Anayilemba motere:
9 De, der dengang skrev, var Statholderen Rehum og Skriveren Sjimsjaj og alle deres andre Embedsbrødre, Diniterne, Afarsatkiterne, Tarpeliterne, Afaresiterne, Arkiterne, Babylonerne,
Kalata yochokera kwa Rehumu, mkulu wa gulu lankhondo, mlembi Simisai ndi anzawo awa: oweruza, nduna, akuluakulu ena, anthu a ku Peresiya, Ereki, Babuloni, Susa mʼdziko la Elamu,
10 Susaniterne, Dehaviterne, Elamiterne og de andre Folk, som den store og navnkundige Asenappar havde ført bort og ladet bosætte sig i Samarias Byer og andensteds hinsides Floden, og så videre.
ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.
11 Dette er en Afskrift af Brevet, de sendte ham: "Til Kong Artaxerxes. Dine Trælle, Folkene hinsides Floden, og så videre:
Mawu a mʼkalata ya kwa Aritasasita anali awa: Kwa mfumu Aritasasita: Kuchokera kwa atumiki anu, anthu a kutsidya kwa Yufurate:
12 Det være Kongen kundgjort, at Jøderne, som drog op til os fra dig, er kommet til Jerusalem; de er i Færd med at genopbygge denne oprørske og onde By; de genopfører Murene og udbedrer Grunden.
Amfumu tati mudziwe kuti Ayuda amene anabwera kuno kuchokera kwanuko apita ku Yerusalemu ndipo akumanganso mzinda wa anthu owukira ndi oyipa uja. Akumaliza makoma ake ndipo akukonzanso maziko.
13 Men nu være det Kongen kundgjort, at hvis denne By bygges op og Murene genopføres, så vil de ikke svare Skat, Afgift eller Skyld, og der bliver Skår i Kongens Indtægter.
Kuwonjeza apo amfumu mudziwe kuti ngati amalize kumanganso mzindawu ndi kukonzanso makoma ake, adzaleka kukhoma msonkho, kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko kapena msonkho wina uliwonse, ndipo chuma cha thumba la ufumu chidzachepa.
14 Da vi nu spiser Paladsets Salt, og det ikke sømmer sig for os at se på, at Kongen lider Skade, sender vi herved Bud og lader Kongen det vide,
Popeza tsono ife timadya nawo kwa mfumu sitiyenera tizingoonerera zinthu zochititsa mfumu manyazi. Nʼchifukwa chake tikutumiza uthenga kwa inu a mfumu kuti mudziwe zonse.
15 for at der kan blive set efter i dine Fædres Krønikebog; i den vil du finde og se, at denne By er en oprørsk By, der har voldt Konger og Lande Skade, og at der fra gammel Tid har fundet Opstande Sted i den. Det er Grunden til, at denne By blev ødelagt.
Choncho pachitike kafukufuku mʼbuku la mbiri yakale ya makolo anu. Mʼbuku la mbiri zakale mudzapezamo ndi kuwerenga kuti mzinda umenewu ndi waupandu, wosautsa mafumu ndi nduna zamʼmadera zomwe. Kuyambira kale wakhala ukuwukira ulamuliro uliwonse. Nʼchifukwa chake mzinda umenewu anawuwononga.
16 Så lader vi da Kongen vide, at hvis denne By bygges op og Murerne genopføres, har du ikke mere nogen Besiddelse hinsides Floden!"
Tsono tikukudziwitsani amfumu kuti ngati mzinda umenewu umangidwanso ndi makoma ake nʼkutsirizidwanso ndiye kuti inu simudzalamuliranso chigawo cha patsidya pa Yufurate.
17 Kongen sendte da følgende Svar til Statholderen Rehum, Skriveren Sjimsjaj og alle deres andre Embeddsbrødre, som boede i Samaria og de andre Lande hinsides Floden: "Hilsen, og så videre.
Mfumu inatumiza yankho ili: Mkulu wa gulu lankhondo Rehumu, mlembi Simisai ndi anzanu onse amene akukhala ku Samariya ndi mʼzigawo zina zonse za Patsidya pa Yufurate. Landirani moni.
18 Den Skrivelse, I har sendt mig, er forelæst mig grundigt.
Kalata imene munatumiza ija yawerengedwa bwino lomwe pamaso panga.
19 Og på mit Bud har man set efter og fundet, at denne By fra gammel Tid har sat sig op mod Konger, og at der har fundet Oprør og Opstande Sted i den;
Ine nditalamula kuti afufuze nkhaniyi kwapezekadi kuti mzinda umenewu uli ndi mbiri yowukira mafumu ndi kuti zaupandu ndi zowukira zinkachitikadi mʼmenemo.
20 over Jerusalem har der hersket mægtige Konger, som udstrakte deres Magt over alt hinsides Floden, og til hvem der svaredes Skat, Afgift og Skyld.
Mafumu amphamvu akhala akulamulira Yerusalemu ndi chigawo chonse cha Patsidya pa Yufurate. Iwo ankalandira msonkho ndi kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko pa kanthu kena kalikonse.
21 Giv derfor Ordre til at standse disse Mænd og til, at denne By ikke må genopbygges, før der kommer Befaling fra mig;
Tsopano inu khazikitsani lamulo kuti anthu amenewo asiye ntchitoyo, asamangenso mzindawo mpaka ine nditalamula
22 og tag eder vel i Vare for at vise Forsømmelighed i denne Sag, at ikke der skal lides store Tab til Skade for Kongerne!
Musachedwe kuchita zimenezi. Kodi ine ndingalole bwanji kuti zowononga zotere zikule ndi kupweteka ine mfumu?
23 Så snart Afskriften af denne Skrivelse fra Kong Artaxerxes var blevet læst for Rehum, Skriveren Sjimsjaj og deres Embedsbrødre, begav de sig uopholdelig til Jøderne i Jerusalem og tvang dem med Magt til at standse Arbejdet.
Kalata ya mfumu Aritasasitayi itangowerengedwa pamaso pa Rehumu ndi Simisai mlembi uja, ndi anzawo onse, iwo anapita msangamsanga ku Yerusalemu kukawaletsa Ayuda aja mwamphamvu kuti asapitirire ntchito yawo.
24 Så standsede Arbejdet på Guds Hus i Jerusalem, og det hvilede til Perserkongen Darius's andet Regeringsår.
Motero ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu inayimitsidwa mpaka chaka cha chiwiri cha ulamuliro wa Dariyo mfumu ya ku Perisiya.

< Ezra 4 >