< Ezekiel 39 >

1 Du, Menneskesøn, Profeter mod Gog og sig: Så siger den Herre HERREN. Se, Jeg kommer over dig, Gog, Fyrste over Rosj, Mesjek og Tubal!
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 Jeg vender dig, leder dig og fører dig op fra det yderste Nord og bringer dig til Israels Bjerge.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 Så slår jeg Buen ud af din venstre Hånd og lader Pilene falde ud af din højre.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 På Israels Bjerge skal du falde, du og alle dine Hobe og Folkeslagene, der følger dig; jeg giver dig til Føde for alle Hånde Rovfugle og Markens vilde Dyr.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 I åben Mark skal du falde, så sandt jeg har talet, lyder det fra den Herre HERREN.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 Og jeg sætter Ild på Magog og på de fjerne Strandes trygge Indbyggere; og de skal kende, at jeg er HERREN.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 Mit hellige Navn kundgør jeg midt i mit Folk Israel, og jeg vil ikke mere vanhellige mit hellige Navn; og Folkene skal kende, at jeg er HERREN, den Hellige i Israel.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Se, det kommer, det skal ske, lyder det fra den Herre HERREN; det er Dagen, jeg har talet om.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Så skal Indbyggerne i Israels Byer gå ud og gøre Ild på og tænde op med Rustninger, små og store Skjolde, Buer, Pile, Håndstave og Spyd; og de skal bruge det til at gøre Ild med i syv År.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 De skal ikke hente Træ i Marken eller hugge Brænde i Skovene, men gøre Ild på med Rustningerne. De skal plyndre dem, de plyndredes af, og hærge dem, de hærgedes af, lyder det fra den Herre HERREN.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 Og på hin Dag giver jeg Gog et Gravsted i Israel, Vandringsmændenes dal østen for Havet, og den skal spærre Vejen for Vandringsmænd; der skal de jorde Gog og hele hans larmende Hob og kalde Stedet: Gogs larmende Hobs dal.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 Israels Hus skal have hele syv Måneder til at jorde dem og således rense Landet.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Alt folket i Landet skal jorde dem, og det skal tjene til deres Ros, på den Dag jeg herliggør mig, lyder det fra den Herre HERREN.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 Man skal udvælge fast Mandskab til at drage Landet rundt og søge efter dem, der er blevet tilbage ud over Landet, for at rense det; når syv Måneder er gået, skal de skride til at søge;
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 og når de vandrer Landet rundt og en får Øje på Menneskeknogler, skal han sætte et Mærke derved, for at Graverne kan jorde dem i Gogs larmende Hobs Dal;
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 også skal en By have Navnet Hamona". Således skal de rense Landet.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Og du, Menneskesøn! Så siger den Herre HERREN: Sig til alle Fugle og alle Markens vilde Dyr: Saml eder og kom hid, kom sammen alle Vegne fra til mit Slagtoffer, som jeg slagter for eder, et vældigt Slagtoffer på Israels Bjerge; I skal æde Kød og drikke Blod!
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 Kød af Helte skal I æde, Blod af Jordens Fyrster skal I drikke, Vædre, Får, Bukke og Tyre, alle fedet i Basan.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 I skal æde eder mætte i Fedt og drikke eder drukne i Blod af mit Slagtoffer, som jeg slagter for eder.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 I skal mætte eder ved mit Bord med Køreheste og Rytterheste, Helte og alle Hånde Krigsfolk, lyder det fra den Herre HERREN.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 Jeg åbenbarer min Herlighed blandt Folkene, og alle Folkene skal skue den Dom, jeg fuldbyrder, og min Hånd, som jeg lægger på dem.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 Israels Hus skal kende, at jeg, HERREN, er deres Gud fra hin Dag og fremdeles;
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 og Folkene skal kende, at Israels Hus vandrede i Landflygtighed for deres Misgerningers Skyld, fordi de var troløse imod mig, så jeg skjulte mit Åsyn for dem og gav dem i deres Fjenders Hånd, hvorfor de alle faldt for Sværdet.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 Efter deres Urenhed og deres Overtrædelser handlede jeg med dem og skjulte mit Åsyn for dem.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Derfor, så siger den Herre HERREN; Nu vil jeg vende Jakobs Skæbne, forbarme mig over alt Israels Hus og være nidkær for mit hellige Navn;
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 og de skal glemme deres Skændsel og al den Troløshed, de viste mig, når de bor trygt i deres Land, uden at nogen skræmmer,
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 når jeg fører dem tilbage fra Folkeslagene, samler dem fra deres Fjenders Lande og helliger mig på dem for mange Folks Øjne.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 Og de skal kende, at jeg er HERREN deres Gud, når jeg efter at have ført dem i Landflygtighed blandt Folkene samler dem i deres Land uden at lade nogen af dem blive tilbage derude
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 og ikke mere skjuler mit Åsyn for dem, da jeg har udgydt min Ånd over Israels Hus, lyder det fra den Herre HERREN.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 39 >