< 2 Mosebog 1 >

1 Dette er Navnene på Israels Sønner, der sammen med Jakob kom til Ægypten med deres Familier:
Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
2 Ruben, Simeon, Levi og Juda,
Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
3 Issakar, Zebulon og Benjamin,
Isakara, Zebuloni, Benjamini;
4 Dan og Naftali, Gad og Aser.
Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
5 Jakobs Efterkommere udgjorde i alt halvfjerdsindstyve, men Josef var i Ægypten.
Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
6 Imidlertid døde Josef og alle hans Brødre og hele dette Slægtled.
Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
7 Men Israeliterne var frugtbare og formerede sig, og de blev mange og overmåde talrige, så at Landet blev fuldt af dem.
Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
8 Da kom der en ny Konge over Ægypten, som ikke vidste noget om Josef;
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
9 og han sagde til sit Folk: "Se, Israels Folk bliver talrigere og stærkere end vi.
Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
10 Velan, lad os gå klogt til Værks imod dem, for at de ikke skal blive for mange; ellers kan det hænde, når vi kommer i Krig, at de går over til vore Modstandere og kæmper mod os og til sidst forlader Landet!"
Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
11 Så satte man Fogeder over dem til at plage dem med Trællearbejde, og de måtte bygge Forrådsbyer for Farao: Pitom og Ra'amses.
Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
12 Men jo mere man plagede dem, des flere blev de, og des mere bredte de sig, så Ægypterne fik Rædsel for Israeliterne.
Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
13 Og Ægypterne tvang Israeliterne til Trællearbejde
ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
14 og gjorde dem Livet bittert ved hårdt Arbejde med Ler og Tegl og alle Hånde Markarbejde, ved alt det Arbejde, de tvang dem til at udføre for sig.
Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
15 Ægypterkongen sagde da til Hebræerkvindernes Jordemødre, af hvilke den ene hed Sjifra, den anden Pua:
Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
16 "Når I forløser Hebræerkvinderne, skal I se godt efter ved Fødselen, og er det et Drengebarn, tag så Livet af det, men er det et Pigebarn, lad det så leve!"
“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
17 Men Jordemødrene frygtede Gud og gjorde ikke, som Ægypterkongen havde befalet dem, men lod Drengebørnene leve.
Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
18 Da lod Ægypterkongen Jordemødrene kalde og sagde til dem: "Hvorfor har I båret eder således ad og ladet Drengebørnene leve?"
Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
19 Men Jordemødrene svarede Farao: "Hebræerkvinderne er ikke som de Ægyptiske Kvinder, de har let ved at føde; inden Jordemoderen kommer til dem, har de allerede født!"
Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
20 Og Gud gjorde vel imod Jordemødrene, og Folket blev stort og såre talrigt;
Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
21 og Gud gav Jordemødrene Afkom, fordi de frygtede ham.
Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
22 Da udstedte Farao den Befaling til hele sit Folk: "Alle Drengebørn, der fødes, skal I kaste i Nilen, men Pigebørnene skal I lade leve!"
Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

< 2 Mosebog 1 >