< 2 Mosebog 8 >

1 Derpå sagde HERREN til Moses: "Gå til Farao og sig til ham: Så siger HERREN: Lad mit Folk rejse, for at de kan dyrke mig!
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 Men hvis du vægrer dig ved at lade dem rejse, se, da vil jeg plage hele dit Land med Frøer;
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 Nilen skal vrimle af Frøer, og de skal kravle op og trænge ind i dit Hus og dit Sovekammer og på dit Leje og i dine Tjeneres og dit Folks Huse, i dine Bagerovne og dine Dejgtruge;
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 ja på dig selv og dit Folk og alle dine Tjenere skal Frøerne kravle op."
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 Da sagde HERREN til Moses: "Sig til Aron: Ræk din Hånd med Staven ud over Floderne, Kanalerne og Dammene og få Frøerne til at kravle op over Ægypten!"
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 Og Aron rakte sin Hånd ud over Ægyptens Vande. Da kravlede Frøerne op og fyldte Ægypten.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 Men Koglerne gjorde det samme ved Hjælp af deres hemmelige Kunster og fik Frøerne til at kravle op over Ægypten.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Da lod Farao Moses og Aron kalde og sagde: "Gå i Forbøn hos HERREN, at han skiller mig og mit Folk af med Frøerne, så vil jeg lade Folket rejse, at de kan ofre til HERREN."
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 Moses svarede Farao: "Du behøver kun at befale over mig! Til hvilken Tid skal jeg gå i Forbøn for dig, dine Tjenere og dit Folk om at få Frøerne bort fra dig og dine Huse, så de kun bliver tilbage i Nilen?"
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 Han svarede: "I Morgen!" Da sagde han: "Det skal ske, som du siger, for at du kan kende, at der ingen er som HERREN vor Gud;
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 Frøerne skal vige bort fra dig, dine Huse, dine Tjenere og dit Folk; kun i Nilen skal de blive tilbage."
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Moses og Aron gik nu bort fra Farao, og Moses råbte til HERREN om at bortrydde Frøerne, som han havde sendt over Farao;
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 og HERREN gjorde, som Moses bad: Frøerne døde i Husene, i Gårdene og på Markerne,
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 og man samlede dem sammen i Dynger, så Landet kom til at stinke deraf.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 Men da Farao så, at han havde fået Luft, forhærdede han sit Hjerte og hørte ikke på dem, således som HERREN havde sagt.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 Derpå sagde HERREN til Moses: "Sig til Aron: Ræk din Stav ud og slå Støvet på Jorden med den, så skal det blive til Myg i hele Ægypten!"
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 Og de gjorde således; Aron udrakte sin Hånd med Staven og slog Støvet på Jorden dermed. Da kom der Myg over Mennesker og Dyr; alt Støvet på Jorden blev til Myg i hele Ægypten.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 Koglerne søgte nu også ved Hjælp af deres hemmelige Kunster at fremkalde Myg, men de magtede det ikke. Og Myggene kom over Mennesker og Dyr.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 Da sagde Koglerne til Farao: "Det er Guds Finger!" Men Faraos Hjerte blev forhærdet, så han ikke hørte på dem, således som HERREN havde sagt.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 Derpå sagde HERREN til Moses: "Træd i Morgen tidlig frem for Farao, når han begiver sig ned til Vandet, og sig til ham: Så siger HERREN: Lad mit Folk rejse, for at de kan dyrke mig!
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 Men hvis du ikke lader mit Folk rejse, se, da sender jeg Bremser over dig, dine Tjenere, dit Folk og dine Huse, og Ægypternes Huse skal blive fulde af Bremser, ja endog Jorden, de bor på;
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 men med Gosens Land, hvor mit Folk bor, vil jeg til den Tid gøre en Undtagelse, så der ingen Bremser kommer, for at du kan kende, at jeg HERREN er i Landet;
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 og jeg vil sætte Skel mellem mit Folk og dit Folk; i Morgen skal dette Tegn ske!"
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 Og HERREN gjorde således: Vældige Bremsesværme trængte ind i Faraos og hans Tjeneres Huse og i hele Ægypten, og Landet hærgedes af Bremserne.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Da lod Farao Moses og Aron kalde og sagde: "Gå hen og bring eders Gud et Offer her i Landet!"
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 Men Moses sagde: "Det går ikke an at gøre således, thi til HERREN vor Gud ofrer vi, hvad der er Ægypterne en Vederstyggelighed; og når vi for Øjnene af Ægypterne ofrer, hvad der er dem en Vederstyggelighed, mon de da ikke stener os?
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 Lad os drage tre Dagsrejser ud i Ørkenen og ofre til HERREN vor Gud, således som han har pålagt os!"
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 Farao sagde: "Jeg vil lade eder rejse hen og ofre til HERREN eders Gud i Ørkenen; kun må I ikke rejse for langt bort; men gå i Forbøn for mig!"
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 Moses svarede: "Se, så snart jeg kommer ud herfra, skal jeg gå i Forbøn hos HERREN, og Bremserne skal vige bort fra Farao, hans Tjenere og hans Folk i Morgen. Blot Farao så ikke igen narrer os og nægter at lade Folket rejse hen og ofre til HERREN!"
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 Derpå gik Moses bort fra Farao og gik i Forbøn hos HERREN.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 Og HERREN gjorde, som Moses bad, og Bremserne veg bort fra Farao, hans Tjenere og hans Folk; der blev ikke en eneste tilbage.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 Men Farao forhærdede også denne Gang sit Hjerte og lod ikke Folket rejse.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

< 2 Mosebog 8 >