< 2 Mosebog 39 >

1 Af det violette og røde Purpurgarn og det karmoisinrøde Garn tilvirkede de Pragtklæderne til Tjenesten i Helligdommen; og de tilvirkede Arons hellige Klæder, således som HERREN havde pålagt Moses.
Anapanga zovala za ansembe, zovala potumikira ku malo wopatulika pogwiritsa ntchito nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira. Anapanganso zovala zopatulika za Aaroni monga momwe Yehova analamulira Mose.
2 De tilvirkede Efoden af Guldtråd, violet og rødt Purpurgarn, karmoisinrødt Garn og tvundet Byssus,
Popanga efodi, iwo anagwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yosalala yofewa.
3 idet de udhamrede Guldet i Plader og skar Pladerne ud i Tråde til at væve ind i det violette og røde Purpurgarn, det karmoisinrøde Garn og det tvundne Byssus ved Kunstvævning.
Anasula golide wopyapyala ndi kumulezaleza kuti alumikize kumodzi ndi nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yosalala yofewa yolukidwa mwaluso.
4 Derpå forsynede de den med Skulderstykker til at hæfte på; den blev hæftet sammen ved begge Hjørner.
Iwo anapanga efodi imene inali ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa, tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
5 Og dens Bælte, som brugtes, når den skulde tages på, var i eet med den og af samme Arbejde, af Guldtråd, violet og rødt Purpurgarn, karmoisinrødt Garn og tvundet Byssus, således som HERREN havde pålagt Moses.
Lamba womangira efodi anali wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Anali nsalu imodzi ndi efodiyo, wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 Derpå tilvirkede de Sjohamstenene, indfattede i Guldfletværk og graverede som Signeter med Israels Sønners Navne;
Iwo anakonza miyala ya onikisi ndi kuyiika mu zoyikamo zake zagolide ndipo anazokota mayina a ana a Israeli monga amachitira pa chidindo.
7 og de fæstede dem på Efodens Skulderstykker, for at Stenene kunde bringe Israels Børn i Minde, således som HERREN havde pålagt Moses.
Kenaka anayimangirira pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli monga momwe Yehova analamulira Mose.
8 Derpå tilvirkede de Brystskjoldet i Kunstvævning på samme Måde som Efoden, af Guldtråd, violet og rødt Purpurgarn, karmoisinrødt Garn og tvundet Byssus;
Iwo anapanga chovala chapachifuwa mwaluso kwambiri. Anachipanga ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
9 det var firkantet, og de lagde Brystskjoldet dobbelt; det var et Spand langt og et Spand bredt, lagt dobbelt.
Kutalika kwake kunali kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, chinali chopinda pawiri.
10 De udstyrede det med fire Rækker Sten: Karneol, Topas og Smaragd i den første Række,
Kenaka anayikapo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba anayika miyala ya rubi, topazi ndi berili;
11 Rubin, Safir og Jaspis i den anden,
mzere wachiwiri anayikapo miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
12 Hyacint, Agat og Ametyst i den tredje,
mzere wachitatu anayikapo miyala ya opera, agate ndi ametisiti;
13 Krysolit, Sjoham og Onyks i den fjerde, omgivne med Guldfletværk i deres Indfatninger.
mzere wachinayi anayikapo miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi anayiyika mu zoyikamo zagolide.
14 Der var tolv Sten, svarende til Israels Sønners Navne, en for hvert Navn; det var graveret Arbejde som Signeter, således at hver Sten bar Navnet på en af de tolv Stammer.
Miyalayo inalipo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse unazokotedwa ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
15 Til Brystskjoldet lavede de snoede Kæder af purt Guld, snoet Arbejde, som når man snor Reb.
Anapanga timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
16 Derpå lavede de to Guldfletværker og to Guldringe og satte disse to Ringe på Brystskjoldets øverste Hjørner,
Anapanganso zoyikamo zake zagolide ndi mphete ziwiri zagolide, ndipo anamangirira mphetezo pa ngodya ziwiri za chovala chapachifuwa.
17 og de to Guldsnore knyttede de i de to Ringe på Brystskjoldets Hjørner;
Anamangirira timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
18 Snorenes anden Ende anbragte de i de to Fletværker og fæstede dem på Forsiden af Efodens Skulderstykker.
Ndipo mbali ina ya timaunyoloto anamangirira pa zoyikapo zake ziwiri zija, ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
19 Og d lavede to andre Guldringe og satte dem på Brystskjoldets to andre Hjørner på den indre Rand, der vendte mod Efoden.
Anapanganso mphete ziwiri zagolide ndipo analumikiza ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
20 Og de lavede endnu to Guldringe og fæstede dem på Efodens to Skulderstykker forneden på Forsiden, hvor den var hæftet sammen med Skulderstykkerne, oven over Efodens Bælte;
Kenaka anapanga mphete zina ziwiri zagolide ndi kuzilumikiza kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
21 og de bandt med Ringene Brystskjoldet fast til Efodens Ringe ved Hjælp af en violet Purpursnor, så at det kom til at sidde oven over Efodens Bælte og ikke kunde løsne sig fra Efoden, som HERREN havde pålagt Moses.
Anamangirira mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi ija monga Yehova analamulira Mose.
22 Derpå tilvirkede de Kåben, som hører til Efoden, i vævet Arbejde, helt og holdent af violet Purpur.
Anayipangira efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo, wolukidwa ndi mmisiri waluso.
23 Midt på havde Kåben en Halsåbning ligesom Halsåbningen på en Panserskjorte, omgivet af en Linning, for at den ikke skulde rives itu,
Mkanjowo unali ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo panali chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
24 og langs Kåbens nederste Kant syede de Granatæbler af violet og rødt Purpurgarn, karmoisinrødt Garn og tvundet Byssus,
Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, analumikiza mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yofewa yosalala ndi yopetedwa bwino yomwe inazungulira mkanjo.
25 og de lavede Bjælder af purt Guld, som de anbragte mellem Granatæblerne langs Kåbens nederste Kant hele Vejen rundt, mellem Granatæblerne,
Ndipo anapanga maberu agolide wabwino kwambiri ndipo analumikiza mozungulira mpendero pakati pa makangadzawo.
26 så at Bjælder og Granatæbler skiftede hele Vejen rundt langs Kåbens nederste Kant, til at bære ved Tjenesten, som HERREN havde pålagt Moses.
Kotero panali mphonje imodzi ndi belu limodzi kuzungulira mpendero wa mkanjo wovala potumikira monga momwe Yehova analamulira Mose.
27 Derpå tilvirkede de Kjortlerne til Aron og hans Sønner af Byssus i vævet Arbejde,
Kwa Aaroni ndi ana ake anawapangira minjiro ya nsalu yofewa yosalala, yolukidwa bwino ndi munthu waluso,
28 Hovedklædet af Byssus, Embedshuerne af Byssus, Linnedbenklæderne af tvundet Byssus,
nduwira ya nsalu yofewa yosalala, lamba wa nsalu yofewa yosalala, womanga mʼmutu, ndi makabudula amʼkati a nsalu yofewa yosalala olukidwa bwino.
29 og Bæltet af tvundet Byssus, violet og rødt Purpurgarn og karmoisinrødt Garn i broget Vævning, som HERREN havde pålagt Moses.
Anapanga lamba wolukidwa bwino wa nsalu yofewa ndi yosalala ya mtundu wa mtambo yapepo ndi yofiira. Ili linaliluso la munthu wopanga zokometsera monga Yehova analamulira Mose.
30 Derpå lavede de Pandepladen, det hellige Diadem, af purt Guld og forsynede den med en Indskrift i graveret Arbejde som ved Signeter: "Helliget HERREN."
Iwo anapanga duwa lagolide wabwino kwambiri ngati chidindo ndipo anazokotapo mawu akuti, Wopatulikira Yehova.
31 Og de fæstede en violet Purpursnor på den til at binde den fast med oven på Hovedklædet, som HERREN havde pålagt Moses.
Kenaka analimangira ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira, monga momwe Yehova analamulira Mose.
32 Således fuldførtes alt Arbejdet ved Åbenbaringsteltets Bolig; og Israeliterne gjorde ganske som HERREN havde pålagt Moses; således gjorde de.
Tsopano ntchito yonse ya tenti ya msonkhano inatha. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
33 Derpå bragte de Boligen til Moses, Teltdækket med alt dets Tilbehør, Knagerne, Brædderne, Tværstængerne, Pillerne og Fodstykkerne,
Kenaka anabweretsa chihema kwa Mose. Tenti ndi zipangizo zake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
34 Dækket af rødfarvede Væderskind og Dækket af Tahasjskind, det indre Forhæng,
chophimba cha chikopa cha nkhosa yayimuna chonyikidwa mu utoto ofiira, chophimba cha chikopa cha akatumbu ndi nsalu zophimba;
35 Vidnesbyrdets Ark med Bærestængerne, Sonedækket,
bokosi la umboni pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake;
36 Bordet med alt dets Tilbehør, Skuebrødene,
tebulo pamodzi ndi zipangizo zake ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
37 Lysestagen af purt Guld med Lamperne, der skulde sættes på den, og alt dens Tilbehør, Olien til Lysestagen,
choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri pamodzi ndi nyale zake ndi zipangizo zake zonse, ndiponso mafuta anyalezo;
38 Guldalteret, Salveolien, den vellugtende Røgelse, Forhænget til Teltets Indgang,
guwa lagolide, mafuta odzozera, lubani onunkhira ndi nsalu yotchinga pa khomo lolowera mu tenti;
39 Kobberalteret med Kobbergitteret, Bærestængerne og alt dets Tilbehør, Vandkummen og Fodstykket,
guwa lamkuwa ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse; beseni ndi miyendo yake;
40 Omhængene til Forgården, Pillerne og Fodstykkerne, Forhænget til Forgårdens Indgang, Rebene og Teltpælene, alt Tilbehør til Tjenesten i Åbenbaringsteltets Bolig,
nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo; zingwe zake ndi zikhomo za tenti; zipangizo zonse za chihema, tenti ya msonkhano;
41 Pragtklæderne til Tjenesten i Helligdommen, de hellige Klæder til Præsten Aron og hans Sønners Klæder til Præstetjenesten.
ndiponso zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.
42 Nøjagtigt som HERREN havde pålagt Moses, udførte Israeliterne hele Arbejdet.
Aisraeli anagwira ntchito yonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
43 Da så Moses hele Arbejdet efter, og se, de havde udført det, som HERREN havde sagt; således havde de utdført det. Og Moses velsignede dem.
Mose anayendera ntchitoyo ndipo anaona kuti anayichita monga momwe Yehova analamulira. Kotero Mose anawadalitsa.

< 2 Mosebog 39 >