< 5 Mosebog 15 >

1 Hvert syvende År skal du holde Friår.
Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
2 Og Friåret skal holdes således: Enhver, der har en Fordring på sin Næste, skal give Afkald derpå; han må ikke kræve sin Næste og sin Broder, når et Friår er udråbt for HERREN.
Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
3 Udlændinge må du kræve; men det, du har til gode hos din Broder, skal du give Afkald på.
Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
4 Dog, der bliver ingen fattige hos dig; thi HERREN din Gud vil rigeligt velsigne dig i det Land, HERREN din Gud vil give dig i Arv og Eje,
Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
5 hvis du blot vil adlyde HERREN din Guds Røst, så du omhyggeligt handler efter alle disse Bud, som jeg i Dag pålægger dig.
Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
6 Thi HERREN din Gud vil velsigne dig, som han lovede dig, og du skal låne ud til mange Folk, men selv skal du ikke låne; og du skal få Magt over mange Folk, men de skal ikke få Magt over dig.
Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
7 Når der findes en fattig hos dig, en af dine Brødre inden dine Porte et steds i dit Land, som HERREN din Gud vil give dig, må du ikke være hårdhjertet og lukke din Hånd for din fattige Broder;
Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
8 men du skal lukke din Hånd op for ham og låne ham, hvad han savner og trænger til.
Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
9 Vogt dig for, at ikke sådan nedrig Tanke kommer op i dig: "Der er ikke længe til det syvende År, Friåret!" så du ser med onde Øjne på din fattige Broder og ikke giver ham noget; thi da vil han råbe til HERREN over dig, og du vil pådrage dig Synd.
Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
10 Men du skal give ham villigt uden at være fortrydelig i dit Hjerte over at skulle give ham; thi for den Sags Skyld vil HERREN din Gud velsigne dig i alt dit Virke, i alt, hvad du tager dig for.
Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
11 Thi der vil aldrig mangle fattige i Landet; derfor byder jeg dig Du skal villigt lukke din Hånd op for din nødlidende og fattige Broder i dit Land.
Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
12 Når en af dine Brødre, en hebraisk Mand eller Kvinde, sælger sig til dig, skal han trælle for dig i seks År, men i det syvende skal du give ham fri.
Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
13 Og når du giver ham fri, må du ikke lade ham gå med tomme Hænder;
Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
14 men du skal give ham rigeligt med af dit Småkvæg og fra din Lo og din Perse; efter som HERREN din Gud velsigner dig, skal du give ham.
Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
15 Du skal komme i Hu, at du selv var Træl i Ægypten, og at HERREN din Gud udløste dig; derfor byder jeg dig dette i dag.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
16 Men hvis han siger til dig: "Jeg vil ikke forlade dig, thi jeg har fået Kærlighed til dig og dit Hus og har det godt hos dig",
Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
17 så skal du tage en Syl og stikke den igennem hans Øre ind i Døren, og så skal han være din Træl for Livstid. Og på samme Måde skal du bære dig ad med din Trælkvinde.
pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
18 Du må ikke være fortrydelig over at skulle give ham fri; thi han har ved sit Arbejde i de seks År ydet dig det dobbelte af en Daglejers Løn; og HERREN vil velsigne dig i alt, hvad du tager dig for.
Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
19 Alle førstefødte Handyr, der fødes dig mellem dit Hornkvæg og Småkvæg, skal du hellige HERREN din Gud; du må hverken bruge det førstefødte af dine Okser til Arbejde eller klippe Ulden af det førstefødte af dine Får.
Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
20 For HERREN din Guds Åsyn skal du sammen med din Husstand fortære det År efter År på det Sted, HERREN udvælger.
Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
21 Men hvis de har en Lyde, hvis de er lamme eller blinde eller har en anden slem Lyde, må du ikke ofre dem til HERREN din Gud.
Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
22 Inden dine Port kan du, både de rene og urene iblandt eder, fortære dem som Gazeller eller Hjorte.
Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
23 Kun Blodet må du ikke nyde; det skal du lade løbe ud på Jorden som Vand.
Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.

< 5 Mosebog 15 >