< Anden Krønikebog 25 >

1 Amazja var fem og tyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede ni og tyve År i Jerusalem. Hans Moder hed Jehoaddan og var fra Jerusalem.
Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
2 Han gjorde, hvad der var ret i HERRENs Øjne, dog ikke med et helt Hjerte.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
3 Da han havde sikret sig Magten, lod han dem af sine Folk dræbe, der havde dræbt hans Fader Kongen,
Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
4 men deres Børn lod han ikke ihjelslå, i Henhold til hvad der står skrevet i Moses's Lovbog, hvor HERREN påbyder: "Fædre skal ikke lide Døden for Børns Skyld, og Børn skal ikke lide Døden for Fædres Skyld. Men enhver skal lide Døden for sin egen Synd."
Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
5 Amazja samlede Judæerne og opstillede dem efter Fædrenehuse under Tusind- og Hundredførerne, hele Juda og Benjamin, og da han mnønstrede dem fra Tyveårsalderen og opefter, fandt han, at de udgjorde 300.000 udvalgte Folk, øvede Krigere, der har Skjold og Spyd.
Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
6 Dertil lejede han i Israel 100.000 dygtige Krigere for 100 Sølvtalenter.
Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
7 Men en Guds Mand kom til ham og sagde: "Israels Hær må ikke følge dig, Konge, thi HERREN er ikke med Israel, ikke med nogen af Efraimiterne;
Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
8 og hvis du mener, at du kan vinde Styrke på den Måde, vil Gud bringe dig til Fald for Fjenden, thi hos Gud er der Kraft til at hjælpe og til at bringe til Fald!"
Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
9 Amazja spurgte den Guds Mand: "Hvad så med de 100 Sølvtalenter, jeg gav de israelitiske Krigsfolk?" Og den Guds Mand svarede: "HERREN kan give dig langt mere end det!"
Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
10 Da udskilte Amazja de Krigsfolk, der var kommet til ham fra Efraim, og lod dem drage hjem; men deres Vrede blussede heftigt op mod Juda, og de vendte hjem i fnysende Vrede.
Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
11 Amazja tog nu Mod til sig og førte sine Krigere til Saltdalen og nedhuggede 10.000 af Se'iriterne;
Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
12 desuden tog Judæerne 10.000 levende til Fange; dem førte de op på Klippens Top og styrtede dem ned derfra, så de alle knustes.
Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
13 Men de Krigsfolk, Amazja havde sendt hjem, så de ikke kom til at følge ham i Krigen, faldt ind i Judas Byer fra Samaria til Bet-Horon, huggede 3.000 af Indbyggerne ned og gjorde stort Bytte.
Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
14 Da Amazja kom hjem fra Sejren over Edomiterne, havde han Se'iriternes Guder med, og han opstillede dem som sine Guder, tilbad dem og tændte Offerild for dem.
Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
15 Da blussede HERRENs Vrede op mod Amazja, og han sendte en Profet til ham, og denne sagde til ham: "Hvorfor søger du dette Folks Guder, som ikke kunde frelse deres Folk af din Hånd?"
Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
16 Men da han talte således, sagde Kongen til ham: "Har man gjort dig til Kongens Rådgiver? Hold inde, ellers bliver du slået ihjel!" Da holdt Profeten inde og sagde: "Jeg indser, at Gud har i Sinde at ødelægge dig, siden du bærer dig således ad og ikke hører mit Råd!"
Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
17 Efter at have overtænkt Sagen sendte Kong Amazja af Juda Bud til Jehus Søn Joahaz's Søn, Kong Joas af Israel, og lod sige: "Kom, lad os se hinanden under Øjne!"
Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
18 Men Kong Joas af Israel sendte Kong Amazja, af Juda det Svar: "Tidselen på Libanon sendte engang det Bud til Cederen på Libanon: Giv min Søn din Datter til Ægte! Men Libanons vilde Dyr løb hen over Tidselen og trampede den ned!
Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
19 Du tænker: Se, jeg har slået Edom! Og det har gjort dig overmodig, så du vil vinde mere Ære. Bliv, hvor du er! Hvorfor vil du udfordre Ulykken og udsætte både dig selv og Juda for Fald?"
Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
20 Men Amazja vilde intet høre, thi Gud føjede det såledesfor at give dem til Pris, fordi de søgte Edoms Guder.
Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
21 Så drog Kong Joas af Israel ud, og han og Kong Amazja af Juda så hinanden under Øjne ved Bet-Sjemesj i Juda;
Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
22 Juda blev slået af Israel, og de flygtede hver til sit.
Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
23 Men Kong Joas af Israel tog Joahaz's Søn Joas's Søn, Kong Amazja af Juda, tifange ved Bet-Sjemesj og førte ham til Jerusalem. Derpå nedrev han Jerusalems Mur på en Strækning af 400 Alen, fra Efraimsporten til Hjørneporten;
Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
24 og han tog alt det Guld og Sølv og alle de Kar, der fandtes i Guds Hus hos Obed-Edom og i Skatkammeret i Kongens Palads; desuden tog han Gidsler og vendte så tilbage til Samaria.
Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
25 Joas's Søn, Kong Amazja af Juda, levede endnu femten År, efter at Joahaz's Søn, Kong Joas at Israel, var død.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
26 Hvad der ellers er at fortælle om Amazja fra først til sidst, står optegnet i Bogen om Judas og Israels Konger.
Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
27 Men ved den Tid Amazja faldt fra HERREN, stiftedes der en Sammensværgelse mod ham i Jerusalem, og han flygtede til Lakisj, men der blev sendt Folk efter ham til Lakisj, og de dræbte ham der.
Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
28 Så løftede man ham op på Heste og jordede ham hos hans Fædre i Davidsbyen.
Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.

< Anden Krønikebog 25 >