< Anden Krønikebog 23 >

1 Men i det syvende År tog Jojada Mod til sig og indgik Pagt med Hundredførerne Azarja, Jerhams Søn, Jisjmael, Johanans Søn, Azarja, Obeds Søn, Ma'aseja, Adajas Søn, og Elisjafat, Zikris Søn.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
2 De drog Juda rundt og samlede Leviterne fra alle Judas Byer og Overhovederne for Israels Fædrenehuse, og de kom så til Jerusalem.
Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
3 Så sluttede hele Forsamlingen i Guds Hus en Pagt med Kongen. Og Jojada sagde til dem: "Se, Kongesønnen skal være Konge efter det Løfte, HERREN har givet om Davids Sønner!
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
4 Og således skal I gøre: Den Tredjedel af eder Præster og Leviter, der rykker ind om Sabbaten, skal tjene som Dørvogtere;
Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
5 den anden Tredjedel skal besætte Kongens Palads og den tredje Jesodporten, medens alt Folket skal besætte Forgården etiI HERRENs Hus.
ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
6 Men ingen må betræde HERRENs Hus undtagen Præsterne og de Leviter, der gør Tjeneste; de må gå derind, thi de er hellige; men hele Folket skal holde sig HERRENs Forskrift efterrettelig.
Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
7 Så skal Leviterne, alle med Våben i Hånd, slutte Kreds om Kongen, og enhver, der nærmer sig Templet, skal dræbes. Således skal I være om Kongen, når han går ind, og når han går ud."
Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
8 Leviterne og alle Judæerne gjorde alt, hvad Præsten Jojada havde påbudt, idet de tog hver sine Folk, både dem, der rykkede ud, og dem, der rykkede ind om Sabbaten, thi Præsten Jojada gav ikke Skifterne Orlov.
Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
9 Og Præsten Jojada gav Hundredførerne Spydene og de små og store Skjolde, som havde tilhørt Kong David og var i Guds Hus.
Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
10 Derpå opstillede han alt Folket, alle med Spyd i Hånd, fra Templets Sydside til Nordsiden, hen til Alteret og derfra igen hen til Templet, rundt om Kongen.
Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
11 Så førte de Kongesønnen ud, satte Kronen og Vidnesbyrdet på ham; derefter udråbte de ham til Konge, og Jojada og hans Sønner salvede ham og råbte: "Kongen leve!"
Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
12 Da Atalja hørte Larmen af Folket, som løb og jublede for Kongen, gik hun hen til Folket i HERRENs Hus,
Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
13 og der så hun Kongen stå på sin Plads ved Indgangen og Øversterne og Trompetblæserne ved Siden af, medens alt Folket fra Landet jublede og blæste i Trompeterne, og Sangerne med deres Instrumenter ledede Lovsangen. Da sønderrev Atalja sine Klæder og råbte: "Forræderi, Forræderi!"
Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
14 Men Præsten Jojada bød Hundredførerne, Hærens Befalingsmænd: "Før hende uden for Forgårdene og hug enhver ned, der følger hende, thi - sagde Præsten - I må ikke dræbe hende i HERRENs Hus!"
Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
15 Så greb de hende, og da hun ad Hesteporten var kommet til Kongens Palads, dræbte de hende der.
choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
16 Men Jojada sluttede Pagt mellem sig og hele Folket og Kongen om, at de skulde være HERRENS folk.
Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
17 Og alt Folket begav sig til Ba'als Hus og nedbrød det; Altrene og Billederne huggede de i Stykker, og Ba'als Præst Mattan dræbte deforan Altrene.
Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
18 Derpå satte Jojada Vagtposter ved HERRENs Hus under Ledelse af Præsterne og Leviterne, som David havde tildelt HERRENs Hus, for at de skulde bringe HERREN Brændofre, som det er foreskrevet i Mose Lov, under Jubel og Sang efter Davids Anordning;
Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
19 og han opstillede Dørvogterne ved HERRENs Hus's Porte, for at ingen, der i nogen Måde var uren, skulde gå derind;
Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
20 og han tog Hundredførerne og Stormændene og Folkets overordnede og alt Folket fra Landet og førte Kongen ned fra HERRENs Hus; de gik igennem Øvreporten til Kongens Palads og satte Kongen på Kongetronen.
Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
21 Da glædede alt Folket fra Landet sig, og Byen holdt sig rolig. Men Atalja huggede de ned.
ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.

< Anden Krønikebog 23 >