< 1 Mosebog 12 >

1 Og Herren sagde til Abram: Gak du ud af dit Land og fra din Slægt og af din Faders Hus til det Land, som jeg vil vise dig.
Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.
2 Og jeg vil gøre dig til et stort Folk og velsigne dig og gøre dit Navn stort, og vær en Velsignelse.
“Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu ndipo ndidzakudalitsa; ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.
3 Og jeg vil velsigne dem, som velsigne dig, og den, som forbander dig, vil jeg forbande; og i dig skulle alle Slægter paa Jorden velsignes.
Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe, ndi kutemberera amene adzatemberera iwe; ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iwe.”
4 Og Abram gik, ligesom Herren havde sagt til ham, og Lot gik med ham; og Abram var halvfjerdsindstyve Aar og fem Aar gammel, der han uddrog af Haran.
Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75.
5 Saa tog Abram Sarai sin Hustru og Lot sin Broders Søn og al deres Ejendom, som de ejede, og de Folk, som de havde forskaffet sig i Haran, og de droge ud for at rejse til Kanaans Land, og de kom til Kanaans Land.
Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.
6 Og Abram drog igennem Landet til det Sted Sikem indtil More Lund; og Kananiten var da i Landet.
Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo.
7 Og Herren aabenbaredes for Abram og sagde: Dit Afkom vil jeg give dette Land; og han byggede der et Alter for Herren, som aabenbaredes for ham.
Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.
8 Og han brød op derfra til Bjerget Østen for Bethel og udslog sit Telt, saa Bethel var mod Vesten og Ai mod Østen; og han byggede der et Alter for Herren og paakaldte Herrens Navn.
Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo.
9 Og Abram rejste videre og vandrede mod Sønden.
Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.
10 Og der var Hunger i Landet, og Abram drog ned til Ægypten at leve som fremmed der; thi Hungeren var svar i Landet.
Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri.
11 Og det skete, der han nærmede sig at komme til Ægypten, sagde han til Sarai sin Hustru: Se nu, jeg ved, at du er en dejlig Kvinde at se til.
Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri.
12 Og det vil ske, naar Ægypterne se dig og sige: denne er hans Hustru, at de slaa mig ihjel og lade dig leve.
Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo.
13 Kære, sig, at du er min Søster, at det kan gaa mig vel for din Skyld, og min Sjæl maa leve formedelst dig.
Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”
14 Og det skete, der Abram kom til Ægypten, da saa Ægypterne Kvinden, at hun var meget dejlig.
Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi.
15 Og Faraos Fyrster saa hende og roste hende for Farao, og Kvinden blev ført til Faraos Hus.
Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao.
16 Og han gjorde Abram godt for hendes Skyld; og han fik Faar og Kvæg og Asener og Svende og Tjenestepiger og Aseninder og Kameler.
Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.
17 Og Herren slog Farao og hans Hus med store Plager for Sarai, Abrams Hustrus, Skyld.
Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu.
18 Da kaldte Farao ad Abram og sagde: Hvi har du gjort mig dette? hvi gav du mig ikke til Kende, at hun er din Hustru?
Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako?
19 Hvorfor sagde du: hun er min Søster? og jeg tog hende mig til Hustru; og nu, se, der er din Hustru, tag hende og gak!
Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!”
20 Og Farao gav sine Mænd Befaling om ham, og de udførte ham og hans Hustru og alt det, han havde.
Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.

< 1 Mosebog 12 >