< Jób 8 >

1 Tedy odpovídaje Bildad Suchský, řekl:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Dokudž mluviti budeš takové věci, a slova úst tvých budou jako vítr násilný?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Což by Bůh silný neprávě soudil, a Všemohoucí což by převracel spravedlnost?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Synové zajisté tvoji že zhřešili proti němu, proto pustil je po nepravosti jejich.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Kdybys ty opravdově hledal Boha silného, a Všemohoucímu se modlil,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 A byl čistý a upřímý: jistě žeť by se hned probudil k tobě, a napravil by příbytek spravedlnosti tvé.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 A byly by první věci tvé špatné, poslední pak rozmnožily by se náramně.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Nebo vzeptej se, prosím, věku starého, a nastroj se k zpytování otců jejich.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (Myť zajisté včerejší jsme, aniž jsme čeho povědomi; k tomu dnové naši jsou jako stín na zemi.)
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Zdaliž tě oni nenaučí, a nepovědí tobě, a z srdce svého nevynesou-liž slov?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Zdali roste třtí bez bahna? Roste-liž rákosí bez vody?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Nýbrž ještě za zelena, dříve než vytrháno bývá, ano prvé než jaká jiná tráva, usychá.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Tak stezky všech zapomínajících se na Boha silného, tak, pravím, naděje pokrytce zahyne.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Klesne naděje jeho, a doufání jeho jako dům pavouka.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Spolehne-li na dům svůj, neostojí; chytí-li se ho, nezdrží.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Vláhu má před sluncem, tak že z zahrady jeho výstřelkové jeho vynikají.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Při vrchovišti kořenové jeho hustě rostou, i na místech skalnatých rozkládá se.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 A však bývá-li zachvácen z místa svého, až by se ho i odečtlo, řka: Nevidělo jsem tě:
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Tožť ta radost života jeho, a z země jiný vykvetá.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Aj, Bůh silný nepohrdá upřímým, ale nešlechetným ruky nepodává:
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Až i naplní smíchem ústa tvá, a rty tvé plésáním,
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Když nenávidící tebe v hanbu oblečeni budou, a stánku lidí bezbožných nikdež nebude.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Jób 8 >