< 5 Mojžišova 5 >

1 I svolal Mojžíš všecken lid Izraelský, a řekl jim: Slyš, Izraeli, ustanovení a soudy, kteréž já dnes mluvím v uši vaše; naučte se jim, a v skutku jich ostříhejte.
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati: Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata.
2 Hospodin Bůh náš učinil s námi smlouvu na Orébě.
Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu.
3 Ne s otci našimi učinil Hospodin tu smlouvu, ale s námi, kteříž zde jsme nyní my všickni živí.
Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero.
4 Tváří v tvář mluvil Hospodin s vámi na té hoře z prostředku ohně,
Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja.
5 (Já jsem pak stál mezi Hospodinem a mezi vámi toho času, abych oznámil vám řeč Hospodinovu; nebo jste se báli ohně, a nevstoupili jste na horu), řka:
(Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:
6 Já jsem Hospodin Bůh tvůj, kterýž jsem tě vyvedl z země Egyptské z domu služby.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
7 Nebudeš míti bohů jiných přede mnou.
“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.
8 Neučiníš sobě rytiny, ani jakého podobenství těch věcí, kteréž jsou na nebi svrchu, ani těch, kteréž na zemi dole, ani těch, kteréž jsou u vodách pod zemí.
“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
9 Nebudeš se jim klaněti, ani jich ctíti. Nebo já jsem Hospodin Bůh tvůj, Bůh silný, horlivý, navštěvující nepravost otců na synech do třetího i čtvrtého pokolení těch, kteříž nenávidí mne,
Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane,
10 A činící milosrdenství nad tisíci těch, kteříž mne milují, a ostříhají přikázaní mých.
koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.
11 Nevezmeš jména Hospodina Boha svého nadarmo, neboť nenechá bez pomsty Hospodin toho, kdož by bral jméno jeho nadarmo.
“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
12 Ostříhej dne sobotního, abys jej světil, jakož přikázal tobě Hospodin Bůh tvůj.
“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira.
13 Šest dní pracovati budeš, a dělati všeliké dílo své;
Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi,
14 Ale dne sedmého odpočinutí jest Hospodina Boha tvého. Nebudeš dělati žádného díla, ty i syn tvůj i dcera tvá, i služebník tvůj i děvka tvá, vůl i osel tvůj i všeliké hovado tvé, i příchozí tvůj, kterýž jest v branách tvých, aby odpočinul služebník tvůj a děvka tvá jako i ty.
koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo.
15 A pamatuj, že jsi byl služebníkem v zemi Egyptské, a vyvedl tě Hospodin Bůh tvůj odtud v ruce silné, a v rameni vztaženém. Protož přikázal tobě Hospodin Bůh tvůj, abys světil den sváteční.
Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.
16 Cti otce svého i matku svou, jakož přikázal tobě Hospodin Bůh tvůj, aby se prodleli dnové tvoji, a aby tobě dobře bylo na zemi, kterouž Hospodin Bůh tvůj dá tobě.
“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
17 Nezabiješ.
“Usaphe.
18 Nesesmilníš.
“Usachite chigololo.
19 Nepokradeš.
“Usabe.
20 Nepromluvíš proti bližnímu svému křivého svědectví.
“Usapereke umboni womunamizira mnzako.
21 Nepožádáš manželky bližního svého, aniž požádáš domu bližního svého, pole jeho, neb služebníka jeho, aneb děvky jeho, vola jeho neb osla jeho, aneb čehokoli z těch věcí, kteréž jsou bližního tvého.
“Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
22 Ta slova mluvil Hospodin ke všemu shromáždění vašemu na hoře z prostředku ohně, oblaku a mrákoty, hlasem velikým, a nepřidal nic více, a napsal je na dvou dskách kamenných, kteréž mně dal.
Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.
23 Vy pak když jste uslyšeli hlas z prostředku tmy, (nebo hora ohněm hořela, ) přistoupili jste ke mně všickni vůdcové pokolení vašich a starší vaši,
Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine.
24 A řekli jste: Ej, ukázal nám Hospodin Bůh náš slávu svou a velikost svou, a slyšeli jsme hlas jeho z prostředku ohně; dnešního dne viděli jsme, že Bůh mluvil s člověkem, a on živ zůstal.
Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye.
25 Protož nyní proč máme zemříti? Nebo sežral by nás oheň veliký tento; jestli více slyšeti budeme hlas Hospodina Boha našeho, zemřeme.
Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu.
26 Nebo co jest všeliké tělo, aby slyše hlas Boha živého mluvícího z prostředku ohně, jako my, mělo živo býti?
Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo?
27 Přistup ty a slyš všecky věci, kteréž mluviti bude Hospodin Bůh náš; potom ty mluviti budeš nám, což by koli řekl tobě Hospodin Bůh náš, a my slyšeti i činiti budeme.
Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”
28 Uslyšev pak Hospodin hlas řečí vašich, když jste mluvili ke mně, řekl mi Hospodin: Slyšel jsem hlas řeči lidu tohoto, kterouž mluvili tobě. Cožkoli mluvili, dobřeť jsou mluvili.
Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino.
29 Ó kdyby bylo jejich srdce takové, aby se báli mne a ostříhali přikázaní mých po všeliký čas, aby jim dobře bylo i synům jejich na věky!
Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.
30 Jdi, rci jim: Navraťte se k stanům vašim.
“Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo.
31 Ty pak stůj tuto při mně, a oznámím tobě všecka přikázaní, ustanovení i soudy, kterýmž je učiti budeš, aby je činili v zemi, kterouž já dávám jim, aby jí dědičně vládli.
Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”
32 Hleďtež tedy, abyste činili, jakž přikázal vám Hospodin Bůh váš; neuchylujte se na pravo ani na levo.
Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.
33 Po vší té cestě, kterouž vám přikázal Hospodin Bůh váš, choditi budete, abyste živi byli, a dobře bylo vám, a abyste prodlili dnů na zemi, kterouž dědičně obdržíte.
Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.

< 5 Mojžišova 5 >