< 2 Kronická 11 >

1 Když pak přijel Roboám do Jeruzaléma, shromáždil dům Judův a Beniaminův, sto a osmdesáte tisíc výborných bojovníků, aby bojovali proti Izraelovi, a aby zase obráceno bylo království k Roboámovi.
Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
2 Tedy stala se řeč Hospodinova k Semaiášovi, muži Božímu, řkoucí:
Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
3 Pověz Roboámovi synu Šalomounovu, králi Judskému, a všemu lidu Izraelskému, kterýž jest v pokolení Judově a Beniaminově, řka:
“Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
4 Takto praví Hospodin: Netáhněte a nebojujte proti bratřím svým, navraťte se jeden každý do domu svého; nebo ode mne stala se věc tato. I uposlechli rozkazu Hospodinova, a navrátili se, aby netáhli proti Jeroboámovi.
‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
5 I bydlil Roboám v Jeruzalémě, a vzdělal města hrazená v Judstvu.
Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
6 A vzdělal Betlém, Etam. a Tekoe,
Betelehemu, Etamu, Tekowa,
7 Betsur, Socho a Adulam,
Beti Zuri, Soko, Adulamu,
8 Gát, Maresa a Zif,
Gati, Maresa, Zifi,
9 Adoraim, Lachis a Azeka,
Adoraimu, Lakisi, Azeka,
10 Zaraha, Aialon a Hebron, kteráž byla v pokolení Judově a Beniaminově města hrazená.
Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
11 A když upevnil města hrazená, osadil v nich knížata, a zdělal špižírny k potravám, k oleji a vínu.
Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
12 A v jednom každém městě složil štíty a kopí, a opatřil ta města velmi dobře, a tak kraloval nad Judou a Beniaminem.
Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
13 Kněží také a Levítové, kteříž byli ve všem Izraeli, postavili se k němu ze všech končin svých.
Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
14 Opustili byli zajisté Levítové předměstí svá i vládařství svá, a odebrali se do Judstva a do Jeruzaléma, (proto, že je zavrhl Jeroboám a synové jeho, aby v úřadu kněžském nesloužili Hospodinu.
Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
15 A nařídil sobě kněží k sloužení po výsostech ďáblům a telatům, kterýchž byl nadělal).
Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
16 A za nimi ze všech pokolení Izraelských ti, kteříž oddali srdce své k hledání Hospodina Boha Izraelského, přišli do Jeruzaléma, aby obětovali Hospodinu Bohu otců svých.
Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
17 A tak utvrdili království Judské, a zsilili Roboáma syna Šalomounova za tři léta, a po ta tři léta chodili po cestě Davidově a Šalomounově.
Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
18 Potom pojal sobě Roboám ženu, Mahalat, dceru Jerimota syna Davidova, a Abichail, dceru Eliaba syna Izai.
Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
19 Kteráž mu zplodila syny: Jeusa a Semariáše a Zahama.
Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
20 A po té pojal Maachu dceru Absolonovu, kteráž mu porodila Abiáše, Attaie, Zizu a Selomita.
Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
21 Ale miloval Roboám Maachu dceru Absolonovu, nade všecky ženy i ženiny své; nebo byl pojal žen osmnáct, a ženin šedesát, a zplodil dvadceti a osm synů a šedesáte dcer.
Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
22 Ustanovil pak Roboám Abiáše syna Maachy za kníže a vývodu mezi bratřími jeho; nebo myslil ho ustanoviti králem.
Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
23 A opatrnosti užívaje, rozsadil všecky jiné syny své po všech krajích Judových a Beniaminových, ve všech městech ohrazených, i dal jim potravy hojně, a nabral jim mnoho žen.
Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.

< 2 Kronická 11 >