< Jošua 19 >

1 Drugi ždrijeb izađe za Šimuna, za pleme sinova Šimunovih po porodicama njihovim: njihova je baština bila usred sinova Judinih.
Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
2 Dodijeljena im je kao baština: Beer Šeba, Šeba, Molada;
Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
3 Hasar Šual, Bala, Esem;
Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
4 Eltolad, Betul, Horma,
Elitoladi, Betuli, Horima,
5 Siklag, Bet-Hamarkabot, Hasar Susa,
Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
6 Bet-Lebaot i Šaruhen: trinaest gradova i njihova sela.
Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
7 Ajin, Rimon, Eter i Ašan: četiri grada s njihovim selima.
Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
8 I sva naselja što su oko tih gradova, do Baalat Beera, Ramat Negeba. To je baština plemena sinova Šimunovih po porodicama njihovim.
Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
9 Baština je sinova Šimunovih bila od dijela sinova Judinih, jer dio dodijeljen sinovima Judinim bijaše za njih prevelik. Zato su sinovi Šimunovi dobili svoju baštinu usred njihova područja.
Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
10 Treći ždrijeb izađe za sinove Zebulunove po porodicama njihovim: njihovo je područje sezalo do Sarida,
Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
11 odakle im se međa na zapadu penjala do Marale, doticala Dabešet i dopirala do potoka koji je nasuprot Jokneamu.
Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
12 Od Sarida je međa okretala prema istoku, sve do međe Kislot Tabora, odakle je izlazila do Dabrata i uspinjala se do Jafije.
Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
13 A odatle je išla opet prema istoku, na Git Hefer i na Ita Kasin, izlazila na Rimon i vraćala se do Nee.
Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
14 Onda je okretala sa sjevera oko Hanatona i završavala se u dolini Jiftah-Elu.
Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
15 Pa Katat, Nahalal, Šimron, Jidalu i Betlehem: dvanaest gradova s njihovim selima.
Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
16 To je bila baština sinova Zebulunovih po porodicama njihovim: ti gradovi s njihovim selima.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
17 Četvrti je ždrijeb izašao za Jisakara, za sinove Jisakarove po njihovim porodicama.
Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
18 A posjed im je bio: Jizreel, Hakesulot, Šunem;
Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
19 Hafarajim, Šion, Anaharat;
Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
20 Harabit, Kišjon, Ebes;
Rabiti, Kisoni, Ebezi,
21 Remet i En-Ganim, En-Hada i Bet-Pases.
Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
22 Potom međa dotiče Tabor, Šahasimu i Bet-Šemeš i izlazi na Jordan: šesnaest gradova s njihovim selima.
Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
23 To je baština plemena sinova Jisakarovih po porodicama njihovim: ti gradovi s njihovim selima.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
24 Peti ždrijeb iziđe za pleme sinova Ašerovih po njihovim porodicama.
Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
25 Njihova je zemlja bila: Helkat, Hali, Beten, Akšaf,
Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
26 Alamelek, Amad, Mišal. Na zapadu je međa doticala Karmel i Šihor Libnat.
Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
27 Zatim je okretala prema sunčanom istoku do Bet-Dagona i doticala se Zebuluna i doline Jiftahela sa sjevera; protezala se dalje Bet-Haemekom i Neielom i dosezala slijeva Kabul,
Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
28 pa Abdon, Rehob, Hamon i Kanu sve do Velikog Sidona.
Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
29 Međa je tada zavijala prema Rami i do tvrdoga grada Tira te je okretala prema Hosi i izlazila na more. Obuhvaćala je Mehaleb, Akzib,
Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
30 Ako, Afek i Rehob: dvadeset i dva grada s njihovim selima.
Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
31 To je baština plemena sinova Ašerovih po porodicama njihovim: ti gradovi i njihova sela.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
32 Šesti ždrijeb izađe za sinove Naftalijeve po njihovim porodicama.
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
33 Njihova međa ide od Helefa i od Hrasta u Saananimu, od Adami Hanekeba i Jabneela do Lakuma i izbija na Jordan.
Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
34 Potom međa okreće na zapad k Aznot Taboru i pruža se odande prema Hukoku; na jugu se dotiče Zebuluna, na zapadu Ašera, na istoku Jordana.
Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
35 Utvrđeni gradovi bijahu Hasidim, Ser, Hamat, Rakat, Kineret;
Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
36 Adama, Rama, Hasor,
Adama, Rama, Hazori,
37 Kedeš, Edrej, En-Hasor;
Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
38 Jiron, Migdal-El, Horem, Bet-Anat, Bet-Šemeš: devetnaest gradova s njihovim selima.
Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
39 To je baština plemena Naftalijevih sinova po porodicama njihovim: ti gradovi i njihova sela.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
40 Izađe sedmi ždrijeb za pleme sinova Danovih po porodicama njihovim.
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
41 Područje baštine njihove bilo je: Sora, Eštaol, Ir Šemeš,
Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
42 Šaalabin, Ajalon, Jitla,
Saalabini, Ayaloni, Itira,
43 Elon, Timna, Ekron,
Eloni, Timna, Ekroni,
44 Elteke, Gibeton, Baalat,
Eliteke, Gibetoni, Baalati,
45 Jehud, Bene-Berak, Gat-Rimon,
Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
46 Me-Hajarkon i Harakon s područjem prema Jafi.
Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
47 Ali područje sinova Danovih bilo je za njih pretijesno; zato udare Danovi sinovi na Lešem, osvoje ga i sve pobiju oštricom mača; zaposjednu grad, nastane se u njemu i Lešem prozovu Dan, po imenu Dana, oca svoga.
Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
48 To je baština plemena sinova Danovih po porodicama njihovim: ti im gradovi i sela njihova.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
49 Kada završe diobu zemlje ždrijebom i utvrde njezine međe, dadu Izraelci Jošui, sinu Nunovu, baštinu u svojoj sredini.
Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
50 Po zapovijedi Jahvinoj dali su mu grad koji je sebi želio: Timnat-Serah u Efrajimovoj gori; on utvrdi taj grad i nastani se u njemu.
Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
51 To su baštine koje su svećenik Eleazar i Jošua, sin Nunov, i glavari izraelskih plemena podijelili ždrijebom među plemena izraelska u Šilu, pred Jahvom, na vratima Šatora sastanka. Tako je zavšena razdioba zemlje.
Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

< Jošua 19 >