< Jakovljeva 4 >

1 Odakle ratovi, odakle borbe među vama? Zar ne odavde: od pohota što vojuju u udovima vašim?
Nʼchiyani chimene chimayambitsa ndewu ndi mapokoso pakati panu? Kodi sizichokera ku zilakolako zimene zimalimbana mʼkati mwanu?
2 Žudite, a nemate; ubijate i hlepite, a ne možete postići; borite se i ratujete. Nemate jer ne ištete.
Mumalakalaka zinthu koma simuzipeza, choncho mumapha. Mumasirira zinthu koma simutha kuzipeza zimene mukufuna, choncho mumakangana ndi kumenyana. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.
3 Ištete, a ne primate jer rđavo ištete: da u pohotama svojim potratite.
Koma ngakhale mumapempha simulandira, chifukwa mumapempha ndi zolinga zoyipa. Mumapempha kuti muzigwiritse ntchito pa zokusangalatsani nokha.
4 Preljubnici! Ne znate li da je prijateljstvo sa svijetom neprijateljstvo prema Bogu? Tko god dakle hoće da bude prijatelj svijeta, promeće se u neprijatelja Božjega.
Inu anthu achigololo, kodi simukudziwa kuti kuchita ubwenzi ndi dziko lapansi ndi kudana ndi Mulungu? Choncho, aliyense wosankha kukhala bwenzi la dziko lapansi amasanduka mdani wa Mulungu.
5 Ili mislite da Pismo uzalud veli: Ljubomorno čezne za duhom što ga nastani u nama?
Kapena mukuganiza kuti Malemba amanena popanda chifukwa kuti Mulungu amafunitsitsa mwansanje mzimu umene Iye anayika kuti uzikhala mwa ife?
6 A daje on i veću milost. Zato govori: Bog se oholima protivi, a poniznima daje milost.
Koma amatipatsa chisomo chochuluka. Nʼchifukwa chake Malemba amati, “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma apereka chisomo kwa odzichepetsa.”
7 Podložite se dakle Bogu! Oduprite se đavlu i pobjeći će od vas!
Dziperekeni nokha kwa Mulungu. Mukaneni Mdierekezi ndipo adzakuthawani.
8 Približite se Bogu i on će se približiti vama! Očistite ruke, grešnici! Očistite srca, dvoličnjaci!
Sendezani kufupi ndi Mulungu ndipo Iye adzasendeza kwa inu. Sambani mʼmanja mwanu, inu anthu ochimwa. Yeretsani mitima yanu, inu anthu okayikira.
9 Zakukajte, protužite, proplačite! Smijeh vaš nek se u plač obrati i radost u žalost!
Chitani chisoni chifukwa cha zimene mwachita, lirani misozi. Kuseka kwanu kusanduke kulira, ndipo chimwemwe chanu chisanduke chisoni.
10 Ponizite se pred Gospodinom i on će vas uzvisiti!
Dzichepetseni pamaso pa Ambuye ndipo Iye adzakukwezani.
11 Ne ogovarajte, braćo, jedni druge! Tko ogovara ili sudi brata svoga, ogovara i sudi Zakon. A sudiš li Zakon, nisi vršitelj nego sudac Zakona.
Abale musamanenane. Aliyense wonenera zoyipa mʼbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo. Pamene muweruza malamulo, ndiye kuti simukusunga malamulowo, koma mukuwaweruza.
12 Jedan je Zakonodavac i Sudac: Onaj koji može spasiti i pogubiti. A tko si ti da sudiš bližnjega?
Pali mmodzi yekha Wopereka Malamulo ndi Woweruza. Ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuwononga. Kodi ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?
13 De sada, vi što govorite: “Danas ili sutra otići ćemo u taj i taj grad, provesti ondje godinu, trgovati i zaraditi”,
Tsono tamverani, inu amene mumati, “Lero kapena mawa tipita ku mzinda wakutiwakuti, tikatha chaka chimodzi tikuchita malonda ndi kupanga ndalama.”
14 a ne znate što će sutra biti. Ta što je vaš život? Dašak ste što se načas pojavi i zatim nestane!
Chifukwa chiyani mukutero? Inu simukudziwa zimene ziti zichitike mawa. Kodi moyo wanu ndi wotani? Inu muli ngati nkhungu imene imangooneka kwa kanthawi kochepa ndipo kenaka ndikuzimirira.
15 Umjesto da govorite: “Htjedne li Gospodin, živjet ćemo i učiniti ovo ili ono”,
Koma inuyo muyenera kunena kuti, “Ambuye akalola, tikadzakhala ndi moyo, tidzachita zakutizakuti.”
16 vi se razmećete svojim hvastanjima! Svako je takvo hvastanje opako.
Koma mmene zililimu mumangodzitama ndi kudzikuza. Kudzitama konse kotereku ndi koyipa.
17 Znati dakle dobro činiti, a ne činiti - grijeh je.
Aliyense amene amadziwa zabwino zimene amayenera kuchita koma osazichita, ndiye kuti wachimwa.

< Jakovljeva 4 >