< Ezekiel 25 >

1 I dođe mi riječ Jahvina:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 “Sine čovječji, okreni lice k sinovima Amonovim te prorokuj protiv njih!
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
3 Reci sinovima Amonovim: 'Poslušajte riječ Jahve Gospoda! Ovako govori Jahve Gospod: Zato što vi klicaste 'ha, ha!' nad mojim Svetištem kad ono bijaše oskvrnuto, i nad zemljom Izraelovom kad ona bijaše opustošena, i nad domom Judinim kad odlažaše u izgnanstvo,
Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
4 predat ću vas, evo, u posjed sinovima Istoka da usred vas razapnu svoje šatore, udare svoja prebivališta. Oni neka jedu tvoje plodove i piju mlijeko tvoje!
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
5 Od Rabe ću pašnjake za deve načiniti, a u zemlji Amonovih sinova torove ću za ovce podići. I znat ćete da sam ja Jahve!'
Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
6 Jer ovako govori Jahve Gospod: 'Zato što si pljeskao rukama i udarao nogama i svom se dušom radovao nad zemljom Izraelovom,
Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
7 ja ću, evo, ruku na te podići i kao plijen te predati narodima! Istrijebit ću te iz narodÄa, iskorijeniti iz zemalja! Zatrijet ću te! I znat ćeš da sam ja Jahve!
Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
8 Ovako govori Jahve Gospod: 'Zato što Moab i Seir govorahu: 'Gle, dom je Judin poput svih naroda',
“Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
9 otkrit ću, evo, obronke moapske, da s kraja na kraj ostane bez gradova što bijahu ukras zemlje: Bet Haješimot, Baal Meon i Kirjatajim.
Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
10 Dat ću ih u posjed sinovima Istoka, neprijateljima Amonaca, da se sinovi Amonovi među narodima više ne spominju!
Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
11 Tako ću izvršiti sud nad Moabom. I znat će da sam ja Jahve!'
Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
12 Ovako govori Jahve Gospod: 'Zato što se Edom osveti domu Judinu i tom se osvetom teško ogriješi,
“Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
13 ovako govori Jahve Gospod: Podići ću ruku na Edom, istrijebit ću iz njega ljude i životinje! Pretvorit ću ga u pustinju: od Temana do Dedana svi će od mača izginuti.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
14 Tako ću se osvetiti Edomu rukom svojega naroda izraelskog. Oni će postupiti s Edomom prema mojem gnjevu i mojoj srdžbi. I spoznat će moju osvetu!' - riječ je Jahve Gospoda.
Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
15 Ovako govori Jahve Gospod: 'Zato što Filistejci izvršiše odmazdu, krvavo se osvećujući s mržnjom u srcu, razarajući sve zbog svojeg neprijateljstva,
“Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
16 ovako govori Jahve Gospod: Evo, podižem ruku na Filistejce, istrijebit ću Kerećane, uništit ću sve što preostane na morskoj obali!
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
17 Tako ću im se strašno osvetiti kaznama jarosnim. I kad im se osvetim, znat će da sam ja Jahve.'”
Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezekiel 25 >