< 2 Kraljevima 21 >

1 Manašeu je bilo dvanaest godina kad se zakraljio. Pedeset i pet godina kraljevao je u Jeruzalemu. Njegova se majka zvala Hefsi-Bah.
Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
2 Činio je što je zlo u Jahvinim očima, povodeći se za gnusobama naroda što ih je Jahve protjerao pred Izraelovim sinovima.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
3 Obnovio je uzvišice što ih bijaše oborio otac mu Ezekija, podigao je žrtvenik Baalu, načinio ašere kako bijaše učinio izraelski kralj Ahab; i stao se klanjati svoj vojsci nebeskoj i služiti joj.
Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
4 Podigao je žrtvenike i u Domu Jahvinu, za koji bijaše rekao Jahve: “U Jeruzalemu će prebivati moje Ime zauvijek.”
Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
5 Sagradio je žrtvenike svoj nebeskoj vojsci u oba predvorja Doma Jahvina.
Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
6 I sinove je svoje proveo kroz oganj. Vračao je, gatao, stvorio bajače i opsjenare, učinio je premnogo zla u očima Jahve i razjarivao ga.
Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
7 Dao je načiniti lik Ašere i posadio ga u Domu, za koji Jahve bijaše rekao Davidu i njegovu sinu Salomonu: “U ovom Domu i u Jeruzalemu, koji sam izabrao među svim izraelskim plemenima, postavit ću svoje Ime zauvijek.
Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
8 Neću više dati da noga Izraelaca uzmakne iz zemlje koju sam dao u baštinu njihovim očevima, samo ako budu držali i provodili u djelo sve što sam im zapovjedio: Zakon što im ga je objavio moj sluga Mojsije.”
Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
9 Ali oni nisu poslušali, Manaše ih je zaveo te su radili još gore nego narodi što ih je Jahve iskorijenio pred Izraelovim sinovima.
Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
10 Tada je Jahve ovako govorio preko slugu svojih proroka:
Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
11 “Zato što je judejski kralj Manaše činio te gnusobe, zato što je učinio više zla nego što su prije njega radili Amorejci i što je zaveo Judejce svojim idolima,
“Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
12 ovako veli Jahve, Bog Izraelov: 'Evo, učinit ću da dođe nevolja na Jeruzalem i Judeju, takva da će zazujati oba uha onima koji o njoj čuju.
Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
13 Nategnut ću nad Jeruzalemom isto uže kao nad Samarijom, isto mjerilo kao nad kućom Ahabovom; zbrisat ću Jeruzalem kao što se briše zdjela pa se tad izvrne.
Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
14 Odbacit ću ostatke svoje baštine, predat ću ih u ruke njihovih neprijatelja; služit će za plijen i grabež svim svojim neprijateljima
Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
15 jer su činili što je zlo u mojim očima jer su izazivali moj gnjev od dana kada su njihovi oci izišli iz Egipta pa sve do danas.'”
chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
16 I mnogo je nedužne krvi prolio Manaše, tako da se njome napunio Jeruzalem od jednoga kraja do drugoga, da se i ne spominje njegov grijeh kojim je zaveo Judu da čini što je zlo u očima Jahvinim.
Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
17 Ostala povijest Manašeova, njegova djela i grijesi koje je počinio, zar sve to nije zapisano u knjizi Ljetopisa judejskih kraljeva?
Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
18 Manaše je počinuo kraj svojih otaca i sahranjen je u vrtu svojeg dvora, u vrtu Uzinu. Sin mu Amon zakralji se mjesto njega.
Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
19 Amonu bijahu dvadeset i dvije godine kad je zavladao, a kraljevao je dvije godine u Jeruzalemu. Njegova se majka zvala Mešulemet, kći Harusova, i bila je iz Jotbe.
Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
20 On je činio što je zlo u očima Jahvinim, kao što je činio njegov otac Manaše.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
21 U svemu je slijedio put svoga oca, služio je idolima kojima je služio i njegov otac i klanjao im se.
Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
22 On je ostavio Jahvu, Boga svojih praotaca, i nije hodio putem Jahvinim.
Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
23 Amonovi se časnici urotiše protiv njega i ubiše kralja u dvoru.
Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
24 Ali je prosti puk pobio sve one koji se bijahu urotili protiv kralja Amona i na njegovo mjesto zakraljio sina mu Jošiju.
Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
25 Ostala povijest Amonova i sve što je činio, zar sve to nije zapisano u knjizi Ljetopisa judejskih kraljeva?
Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
26 Pokopali su ga u grobnicu njegova oca, u vrtu Uzinu, a njegov sin Jošija zakralji se mjesto njega.
Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kraljevima 21 >