< 箴言 4 >

1 眾子啊,要聽父親的教訓, 留心得知聰明。
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 因我所給你們的是好教訓; 不可離棄我的法則。
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 我在父親面前為孝子, 在母親眼中為獨一的嬌兒。
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 父親教訓我說:你心要存記我的言語, 遵守我的命令,便得存活。
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 要得智慧,要得聰明,不可忘記, 也不可偏離我口中的言語。
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 不可離棄智慧,智慧就護衛你; 要愛她,她就保守你。
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 智慧為首; 所以,要得智慧。 在你一切所得之內必得聰明。
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 高舉智慧,她就使你高升; 懷抱智慧,她就使你尊榮。
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 她必將華冠加在你頭上, 把榮冕交給你。
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 我兒,你要聽受我的言語, 就必延年益壽。
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 我已指教你走智慧的道, 引導你行正直的路。
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 你行走,腳步必不致狹窄; 你奔跑,也不致跌倒。
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 要持定訓誨,不可放鬆; 必當謹守,因為它是你的生命。
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 不可行惡人的路; 不要走壞人的道。
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 要躲避,不可經過; 要轉身而去。
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 這等人若不行惡,不得睡覺; 不使人跌倒,睡臥不安;
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 因為他們以奸惡吃餅, 以強暴喝酒。
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 但義人的路好像黎明的光, 越照越明,直到日午。
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 惡人的道好像幽暗, 自己不知因甚麼跌倒。
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 我兒,要留心聽我的言詞, 側耳聽我的話語,
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 都不可離你的眼目, 要存記在你心中。
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 因為得着它的,就得了生命, 又得了醫全體的良藥。
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 你要保守你心,勝過保守一切, 因為一生的果效是由心發出。
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 你要除掉邪僻的口, 棄絕乖謬的嘴。
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 你的眼目要向前正看; 你的眼睛當向前直觀。
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 要修平你腳下的路, 堅定你一切的道。
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 不可偏向左右; 要使你的腳離開邪惡。
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< 箴言 4 >