< 創世記 10 >

1 挪亞的兒子閃、含、雅弗的後代記在下面。洪水以後,他們都生了兒子。
Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2 雅弗的兒子是歌篾、瑪各、瑪代、雅完、土巴、米設、提拉。
Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3 歌篾的兒子是亞實基拿、利法、陀迦瑪。
Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4 雅完的兒子是以利沙、他施、基提、多單。
Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
5 這些人的後裔將各國的地土、海島分開居住,各隨各的方言、宗族立國。
(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6 含的兒子是古實、麥西、弗、迦南。
Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7 古實的兒子是西巴、哈腓拉、撒弗他、拉瑪、撒弗提迦。拉瑪的兒子是示巴、底但。
Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
8 古實又生寧錄,他為世上英雄之首。
Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9 他在耶和華面前是個英勇的獵戶,所以俗語說:「像寧錄在耶和華面前是個英勇的獵戶。」
Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10 他國的起頭是巴別、以力、亞甲、甲尼,都在示拿地。
Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11 他從那地出來往亞述去,建造尼尼微、利河伯、迦拉,
Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12 和尼尼微、迦拉中間的利鮮,這就是那大城。
ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13 麥西生路低人、亞拿米人、利哈比人、拿弗土希人、
Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
14 帕斯魯細人、迦斯路希人、迦斐託人;從迦斐託出來的有非利士人。
Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15 迦南生長子西頓,又生赫
Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
16 和耶布斯人、亞摩利人、革迦撒人、
Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17 希未人、亞基人、西尼人、
Ahivi, Aariki, Asini,
18 亞瓦底人、洗瑪利人、哈馬人,後來迦南的諸族分散了。
Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
19 迦南的境界是從西頓向基拉耳的路上,直到迦薩,又向所多瑪、蛾摩拉、押瑪、洗扁的路上,直到拉沙。
mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20 這就是含的後裔,各隨他們的宗族、方言,所住的地土、邦國。
Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21 雅弗的哥哥閃,是希伯子孫之祖,他也生了兒子。
Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22 閃的兒子是以攔、亞述、亞法撒、路德、亞蘭。
Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23 亞蘭的兒子是烏斯、戶勒、基帖、瑪施。
Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24 亞法撒生沙拉;沙拉生希伯。
Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
25 希伯生了兩個兒子,一個名叫法勒,因為那時人就分地居住;法勒的兄弟名叫約坍。
A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26 約坍生亞摩答、沙列、哈薩瑪非、耶拉、
Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
27 哈多蘭、烏薩、德拉、
Hadoramu, Uzali, Dikila,
28 俄巴路、亞比瑪利、示巴、
Obali, Abimaeli, Seba,
29 阿斐、哈腓拉、約巴,這都是約坍的兒子。
Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30 他們所住的地方是從米沙直到西發東邊的山。
Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31 這就是閃的子孫,各隨他們的宗族、方言,所住的地土、邦國。
Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32 這些都是挪亞三個兒子的宗族,各隨他們的支派立國。洪水以後,他們在地上分為邦國。
Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

< 創世記 10 >