< 诗篇 63 >

1 大卫在犹大旷野的时候,作了这诗。 神啊,你是我的 神, 我要切切地寻求你, 在干旱疲乏无水之地,我渴想你; 我的心切慕你。
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 我在圣所中曾如此瞻仰你, 为要见你的能力和你的荣耀。
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 因你的慈爱比生命更好, 我的嘴唇要颂赞你。
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 我还活的时候要这样称颂你; 我要奉你的名举手。
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 我在床上记念你, 在夜更的时候思想你; 我的心就像饱足了骨髓肥油, 我也要以欢乐的嘴唇赞美你。
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 因为你曾帮助我, 我就在你翅膀的荫下欢呼。
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 我心紧紧地跟随你; 你的右手扶持我。
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 但那些寻索要灭我命的人 必往地底下去;
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 他们必被刀剑所杀, 被野狗所吃。
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 但是王必因 神欢喜。 凡指着他发誓的必要夸口, 因为说谎之人的口必被塞住。
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< 诗篇 63 >