< 诗篇 146 >

1 你们要赞美耶和华! 我的心哪,你要赞美耶和华!
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 我一生要赞美耶和华! 我还活的时候要歌颂我的 神!
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 你们不要倚靠君王,不要倚靠世人; 他一点不能帮助。
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 他的气一断,就归回尘土; 他所打算的,当日就消灭了。
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 以雅各的 神为帮助、 仰望耶和华—他 神的,这人便为有福!
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 耶和华造天、地、海,和其中的万物; 他守诚实,直到永远。
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 他为受屈的伸冤, 赐食物与饥饿的。 耶和华释放被囚的;
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 耶和华开了瞎子的眼睛; 耶和华扶起被压下的人。 耶和华喜爱义人。
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 耶和华保护寄居的, 扶持孤儿和寡妇, 却使恶人的道路弯曲。
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 耶和华要作王,直到永远! 锡安哪,你的 神要作王,直到万代! 你们要赞美耶和华!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< 诗篇 146 >