< 约伯记 41 >
1 你能用鱼钩钓上鳄鱼吗? 能用绳子压下它的舌头吗?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 你能用绳索穿它的鼻子吗? 能用钩穿它的腮骨吗?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 你岂可拿它当雀鸟玩耍吗? 岂可为你的幼女将它拴住吗?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 搭伙的渔夫岂可拿它当货物吗? 能把它分给商人吗?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 你能用倒钩枪扎满它的皮, 能用鱼叉叉满它的头吗?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 你按手在它身上,想与它争战, 就不再这样行吧!
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 没有那么凶猛的人敢惹它。 这样,谁能在我面前站立得住呢?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 谁先给我什么,使我偿还呢? 天下万物都是我的。
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 论到鳄鱼的肢体和其大力,并美好的骨骼, 我不能缄默不言。
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 它以坚固的鳞甲为可夸, 紧紧合闭,封得严密。
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 它打喷嚏就发出光来; 它眼睛好像早晨的光线。
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 从它鼻孔冒出烟来, 如烧开的锅和点着的芦苇。
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 它一起来,勇士都惊恐, 心里慌乱,便都昏迷。
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 人若用刀,用枪,用标枪, 用尖枪扎它,都是无用。
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 凡高大的,它无不藐视; 它在骄傲的水族上作王。
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”