< 约伯记 41 >

1 你能用鱼钩钓上鳄鱼吗? 能用绳子压下它的舌头吗?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 你能用绳索穿它的鼻子吗? 能用钩穿它的腮骨吗?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 它岂向你连连恳求, 说柔和的话吗?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 岂肯与你立约, 使你拿它永远作奴仆吗?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 你岂可拿它当雀鸟玩耍吗? 岂可为你的幼女将它拴住吗?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 搭伙的渔夫岂可拿它当货物吗? 能把它分给商人吗?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 你能用倒钩枪扎满它的皮, 能用鱼叉叉满它的头吗?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 你按手在它身上,想与它争战, 就不再这样行吧!
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 人指望捉拿它是徒然的; 一见它,岂不丧胆吗?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 没有那么凶猛的人敢惹它。 这样,谁能在我面前站立得住呢?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 谁先给我什么,使我偿还呢? 天下万物都是我的。
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 论到鳄鱼的肢体和其大力,并美好的骨骼, 我不能缄默不言。
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 谁能剥它的外衣? 谁能进它上下牙骨之间呢?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 谁能开它的腮颊? 它牙齿四围是可畏的。
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 它以坚固的鳞甲为可夸, 紧紧合闭,封得严密。
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 这鳞甲一一相连, 甚至气不得透入其间,
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 都是互相联络、胶结, 不能分离。
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 它打喷嚏就发出光来; 它眼睛好像早晨的光线。
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 从它口中发出烧着的火把, 与飞迸的火星;
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 从它鼻孔冒出烟来, 如烧开的锅和点着的芦苇。
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 它的气点着煤炭, 有火焰从它口中发出。
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 它颈项中存着劲力; 在它面前的都恐吓蹦跳。
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 它的肉块互相联络, 紧贴其身,不能摇动。
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 它的心结实如石头, 如下磨石那样结实。
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 它一起来,勇士都惊恐, 心里慌乱,便都昏迷。
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 人若用刀,用枪,用标枪, 用尖枪扎它,都是无用。
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 它以铁为干草, 以铜为烂木。
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 箭不能恐吓它使它逃避; 弹石在它看为碎秸。
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 棍棒算为禾秸; 它嗤笑短枪飕的响声。
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 它肚腹下如尖瓦片; 它如钉耙经过淤泥。
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 它使深渊开滚如锅, 使洋海如锅中的膏油。
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 它行的路随后发光, 令人想深渊如同白发。
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 在地上没有像它造的那样, 无所惧怕。
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 凡高大的,它无不藐视; 它在骄傲的水族上作王。
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< 约伯记 41 >